Mutu 21

1 Pamene Yesu na bopunzila bake bana fika pafupi na Yelusalemu kumalo ya Betipagi, ku pili ya Oliva, Yesu anatuma bopunzila bake babili, 2 kubauza kuti, "Endani mu munzi wamene uli pasogolo, pamene mungena muzapeza ka bulu komangilila, naka mwana kake pamozi. Mutu mangusule mutulete kuli ine. 3 Ngati muntu ali onse akufunsani poni pali twemve, imwe mukambe kuti, 'Ambuye ndiye bamene batufuna,' uja muntu azakulekani kuti mututenge mubwele nato." 4 Manje chamene ichi chinachitika kuti vintu vamene anakamba muneneli vikwanilisike. Anakamba kuti, 5 "Mu uzeni mwana mukazi waku Ziyoni kuti, 'Ona, Mfumu yako ibwela kuli iwe, Yozichepesa yakwela bulu-pa kamwana ka bulu, ka mwana ka nyama yonyamula katundu'" 6 Pamene apo bopunzila banayenda naku chita monga mwamene Yesu anabauzila. 7 Banaleta bulu naka mwana ka bulu naku ikapo vovala vabo pali vemve, na Yesu anankala pa vovala. 8 Bambili mu gulu banayanzika vovala vabo pa museu, na benangu bana juba tumitengo naku tuika pa museu. 9 Pamene apo ma gulu ya bantu yana enda pasogolo pa Yesu na baja bamene banali kumukonka uku ndishi bapunda kukamba kuti, "Hosana kuli mwana wa Davide! Niodalisika wamene abwela muzina ya Ambuye! Hosana kumwamba!" 10 Pamene Yesu anangena mu Yelusalemu, muzinda one unagwedeseka naku kamba kuti, "Kansi nindani uyu?" 11 Magulu yanayanka naku kamba kuti, "Uyundiye Yesu muneneli wamene achokela ku Galileya." 12 Yesu anangena mu tempele. Anapisha bonse bamene banali kugulisa naku gula mu tempele, naku pindamula ma tebulo yabaja bochinjisa ndalama na yabaja bamene banali kugulisa nkunda. 13 Anabauza kuti, '"Chinalembewa kuti, 'Nyumba Yanga izaitaniwa kuti ni nyumba yama pempelo,'koma imwe mwaipanga kunkala nyumba yaba kawalala." 14 Pamene apo kunabwela ba mpofu na bolemala mu tempele, anabapolesa. 15 Koma pamene ba bakulu-bakulu nsembe na bolemba bna ona vintu vabwino vamene analikuchita, napamene bana mvela bana bangóno-bangóno mu tempele banali kupunda naku kamba kuti, "Hosana kuli Mwana wa Davide," banakalipa maningi. 16 Banamuuza kuti, "Nanga umvela vamene bakamba?" Yesu anabayanka kuti, "Eeeh! Nanga simunabelenge kuti, 'Kuchokela mukamwa mwa bana bangóno na bana bamene banyonka imwe mwakonza matamando'?" 17 Pamene apo Yesu anabasiya nakuyenda kuchoka mumuzinda nakuyenda ku Betani kwamene anagona. 18 Manje kuseni-seni pamene anabwelela ku muzinda, anamvela njala. 19 Anaona mutengo wa mukuyu mumbali mwa museu, anaenda kuli mutengo uyu naku peka kuti munali chabe ma tepo. Anau uza mutengo uyu kuti, "Musakankalemo chipaso chilichonse muli iwe futi," na pamene apo uja mutengo unayuma. 20 Pamene bopunzila banaona ichi, bana dabwa nakukamba kuti, "Nanga nichani uyu mutengo wayuma pamene apa?" 21 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Zoona niku uzani imwe kuti, ngati muli na chikulupilo nafuti simukaikila, imwe simuzachita chabe chamene chachitika kuli uyu mutengo wa mukuyu, koma imwe muzakamba na kuli iyi pili kuti, 'Tengewa uyende ukaponyewe mu nyanje,' chamene icho chizachitika. 22 Chili chonse chamene imwe mupempa mu pempelo, mokulupilila, muzalandila." 23 Pamene Yesu anafika mu tempele, bakulu-bakulu bansembe na bakulu-bakulu ba bantu banabwela kuli eve pamene anali kupunzisa naku kamba kuti, "Nanga nimpavu zabwanji zamene iwe usebenezesa kuchita ivi, nindani wamene anakupasa mpavu zamene izo?" 24 Yesu anabayanka naku kamba kuti, "Naimwe ine nizakufunsani funso imozi. Ngati muzaniyanka, naine nzaku uzani mpavu zamene ine nisebenzesa kuchita ivi vintu. 25 Kubatiza kwa Yohane-kunachokela kuti? Kumwamba kapena ku bantu?" Banakambisana beka-beka, nakukamba kuti, "Apa ngati takamba kuti, 'Kunachokela kumwamba,' eve azati uza kuti, 'Nanga nichani kansi chamene imwe simuna mukulupilile eve? 26 Koma ngati takamba kuti, 'Ku bantu,' tiyopa gulu, chifukwa bonse bama ona Yohane kunkala muneneli." 27 Banamuyanka Yesu kuti, "Ise sitiziba." Na eve ana bayanka kuti, "Naine sinizaku uzani mpavu zamene ine nisebenzesa kuchita ivi vintu. 28 Nanga imwe muganizapo chani apa? Muntu anali na bana babili. Ana enda kuli uja oyamba naku muuza kuti, 'Mwana wanga, enda ukasebenze mu munda lel.' 29 Uyu mwana anayanka kuti, 'Ine siniza enda,' koma anabwela achinja mutima naku yenda kukasebenza. 30 "Uja muntu anabwela ayenda kuli mwana wake wokonkapo naku muuza chimozi-mozi. Eve anayanka nakukamba kuti, 'Niza enda, atate,' koma sana ende. 31 Ni uti pali aba babili wamene anachita chamene ba tate babo banali kufuna?" Bana yanka kuti, "Uja oyamba." Yesu anabauza kuti, "Zoona niku uzani imwe kuti, baja bamusonko na bachiwelewele bazayambilila kungena mu ufumu wa Mulungu imwe mukalibe kungena. 32 Chifukwa Yohane anabwela kuli mwe minjla yolungama, koma imwe simunamukulupilile. Koma baja bamusonko na bachiwelewele banamu kulupilila. Koma imwe, na pamene imwe muna ona ivi, simuna tembenuke kuti mumukulupilile. 33 "Mvelani mwambo wina. Kunali muntu, mwine wa munda. Anashanga mpesa, naku ikako chochingilizila, anakumba kotwela mpesa uja, na kumanga nyumba ya olonda, naku ibwelekesa pa ndalama kuli bolima mpesa. Anaenda ku ziko ina. 34 Pamene ntawi yo kolola inafika, anatuma bantchito bake kuli balimi ba mpesa kuti batengeko mbali yake ya mpesa. 35 Koma baja bolima mpesa bana batenga bantchito bake, bana menyapo umozi, bana payapo umozi, naku tema myala wina. 36 Futi, uja mwine anatuma benangu bantchito bake, bambili bochila baja boyambilila, koma baja balimi ba mpesa bana bachita chimozi-mozi. 37 Kuchoka apa, mwine anatuma mwana wake kuli beve, kukamba kuti, 'Mwana wanga bazamuyopa.' 38 "Koma pamene baja balimi ba mpesa banaona mwana uja, banakambisana kuti, 'Uyu ndiye azakasala na chuma.' Bwelani, tiyeni timupaye titenge chuma chake.' 39 Banamutenga, banamutaya mu munda wa mpesa naku mupaya. 40 Manje pamene mwine wa munda azakabwela, azakabachita chani baja balimi ba mpesa?" 41 Banamu yanka kuti, "Azaba ononga momvesa chifundo baja bantu boipa munjila yau kali maningi, azabwela abwelekese munda wake kuli benangu balimi ba mpesa, bantu bamene bazamu pasa mbali yake ya vokolola pa ntawi yo enela." 42 Yesu anabauza kuti, "Nanga imwe simuna belenge mumalemba kuti, 'Mwala wamene baja bomanga bana kana wankala ndiye ogwila nyumba yonse. Ichi chinachokela kuli Ambuye, ndipo nichabwino mumenso yatu'? 43 Chifukwa chake nikamba kuli imwe kuti, ufumu wa Mulungu uzapokewa kuli imwe naku pasiwa kuli ziko yamene izabala vipaso vake. 44 Ali onse wamene agwelapo pali uyu mwala azapwanyiwa kunkala tumyala tuongóno tungóno. Koma pali ali onse wamene uzagwela aza onongeka." 45 Pamene bakulu-bakulu ba nsembe na ba Falisi bana mvela izi myambo, banaziba kuti anali kukamba pali beve. 46 Banali kufuna kuti bamugwile, koma banali kuyopa gulu ya bantu, chifukwa bantu banali kumu kamba kuti ni muneneli.