Mutu 20

1 Ufumu wakumwamba uli monga mwine wa munda wamene kuseni-seni anaenda kungenesa bantchito kuti basebenzele mumunda wake wa ma gilepsi. 2 Pamene ana mvelana nabo bantchito kubalipila ndalama imozi pa siku, anabatuma kuyenda kukasebenza mumunda wake wa mpesa. 3 Ana enda nafuti kuma fili koloko yamu mazulo nakupeza benangu bantchito bali imilile pamalo yamalonda. 4 Anabauza kuti, "Naimwe endani mukasebenze mumunda wanga wa mpesa, yamene nizaona kuti ndiye malipilo yanu yabwino ndiye yamene nizakupasani.' Pamene apo bana enda kukasebenza. 5 Anabwela aendako futi pa ntawi ya twelofu koloko na fili koloko ntawi ya muzuba, nakuchita chimozi-mozi. 6 Kamozi futi pantawi ya leveni koloko anaenda nakupeza futi bantu benangu bali imilile banalibe vochita. Anabauza kuti, 'Nanga nichani imwe mwaimilila apa kulibe vamene mungachite?' 7 Banamuyanka kuti, 'Chifukwa kulibe wamene atingenesa ntchito ise.' Anabauza kuti, 'Kansi naimwe endani mu munda wanga mukasebenze.' 8 Pamene inafika ntawi yakumazulo, mwine wa munda uja anauza omulanganila munda kuti, 'Baitane bantchito ubapase ndalama zabo.' 9 "Pamene bantchito baja bamene banangenesewa ntchito pa ntawi ya levini koloko banabwela, ali onse analandila ndalama imozi. 10 Pamene bantchito baja bamene banayambilila kungena ntchito banabwela, banaganizila kuti beve bazalandila ndalama zambili, koma na beve banalandila ndalama imozi chabe. 11 Pamene banalandila malipilo yabo, banadandaula pali mwine wa munda uja. 12 Banakamba kuti, 'Aba bantchito babwela ntawi yokomboka basebenza chabe ola imozi, koma mwaba folesa chimozi-mozi naise, bamene tasebenza ntchto yolimba yalelo na kupya kwa zuba.' 13 "Koma mwine wa munda uja anayanka nakukamba kuti, 'Muzanga iwe, ine sininakulakwile. Nanga sitenze tamvelana iwe naine kuti muzafola ndalama imozi? 14 Ani tenga ndalama yamene iyi ndiye malipilo yako uyende nakuyenda. Ine nasanka kuti na aba bamene bangena ntchito posililiza kuti bafole chimozi-mozi naiwe. 15 Nanga kansi sinilinazo mpavu zochita vilivonse na katundu wanga? Kapena uchita nsanje chifukwa cha mutima wanga opasa? 16 Chifukwa cha ichi uja muntu osilizila azankala oyamba, uja oyamba ndiye azankala osilizila." Ma buku yochilapo yakudala maningi yalibe aya mau yamene yakamba kuti, "Bambili baitaniwa, koma nibangóno bamene basankiwa." 17 Pamene Yesu anali kuyenda ku Yelusalemu, anatenga bopunzila bake bali kumi na babili pambali, munjila muja nakubauza kuti, 18 "Onani, apa tiyenda ku Yelusalemu, kwamene Mwana wa Muntu azapelekewa kuli bakulu ba nsembe na bolemba. Bazamuweluza kuti apaiwe 19 na kumupeleka kuli bantu Bakunja kuti bamunyoze, bamukwapule, naku mupachika pamutanda. Koma pa siku yachitatu azakaukisiwa." 20 Pamene apo mai wa bana ba Zebediya anabwela na bana bake bamuna. Anagwada pansi pali eve naku pempa chintu. 21 Yesu anamuyanka kuti, "Nanga nichani chamene mufuna?" Ana yanka kuti, "Vomelezani kuti bana banga babili aba bakankale, umozi kukwanja yanu yaku manja na wina kukwanja yanu yaku manzele, mu ufumu wanu." 22 Koma Yesu anamuyanka nakukamba uti, "Suziba chamene upempa iwe. Nanga ungakwanise kumwa gome yamene ine nifuna kumwa apa?" Banamuyanka, "Tingakwanise." 23 Anabayanka kuti, "Gome yanga eeeh muzamwa. Koma kunkala ku kwanja yanga ya kwanja na kwanja yanga ya manzele sichintu chakuti ine ningalamule, koma nikwa baja bamene banabakonzela kuli ba Tate banga." 24 Pamene baja bopunzila benangu bali kumi banamvela ichi, banakalipa maningi pali aba babale babili. 25 Koma Yesu anabaitana kuti babwele kuli eve naku bauza kuti, "Imwe muziba kuti basogoleli ba bantu Bakunja bamabafuna kulangiza kuti ndiye basogoleli ku bantu babo, nabaja bantu bozibika bapamwamba bamalangiza mpavu zabo pali beve. 26 Koma kuli imwe visankale njila iyi. Koma, uja muntu wamene afuna kunkala mukulu pali imwe ayenela ankale wantchito kuli imwe, 27 nauja wamene afuna kuti ankale oyamba pakati panu imwe lekani ankale wantchito kuli imwe, 28 monga mwamene Mwana wa Muntu eve sanabwelele kuti bantu bamutumikile, koma kuti atumikile, nakupeleka umoyo wake kunkala cho-ombolelako bantu bambili." 29 Pamene banali kuyena kuchoka ku Yeliko, gulu ikulu inamukonka. 30 Panali ba mpofu babili bamene banali nkale mumbali mwa museu. Pamene banamvela kuti Yesu apita, banapunda kukamba kuti, "Ambuye, Mwana wa Davide, timvelelenikoni chifundo." 31 Koma gulu inabakalipila, kubauza kuti bankale chabe ziii, koma beve banapunda mokwezekelatu mau, "Ambuye, Mwana wa Davide, timvelelenikoni chifundo ise." 32 Yesu anaimilila nakubaitana kukamba kuti, "Nanga nichichani chamene imwe mufuna kuti ine nikuchitiline?" 33 Banamuyanka kuti, "Ambuye, tifuna kuti menso yatu yayambe kuona." 34 Pamene apo Yesu, mogwiliwa nachifundo, anagwila mu menso mwabo. Pamene apo banayamba kuona naku mukonka Yesu.