Mutu 19

1 Pamene Yesu anabwela pambuyo posiliza kukamba aya mau, anachokako ku Galileya nakuyenda kumalo ya Yudeya malo yamene yali kupitilila mumana wa Yodani. 2 Magulu yabantu yanamukonka, anabapolesa kwamene kuja. 3 Ba Falisi banabwela kuli eve, kumuyesa, kumuuza kuti, "Nanga nichovomelesewa kuti mwamuna asiye mukazi wake palibe chifukwa chili chonse?" 4 Yesu anabayanka kuti, "Nanga kansi simunabelenge kuti wamene anabalenga kuchokela kuchiyambi anabalenga mwamuna na mukazi? 5 Eve wamene anabalenga anakamba nafuti kuti, 'chifukwa chake mwamuna azasiya tate wake na mai wake kuyenda kukankala pamozi na mukazi wake, aba babili bazankala tupi imozi.' 6 Chifukwa chake sibantu babili manje koma tupi imozi. Chifukwa chake lekani chamene Mulungu aika pamozi, osavomeleza ali onse kuti apatule." 7 Banakamba kuli eve kuti, "Nanga nichani kansi chamene Mose anatiuza kuti tikazipasa chipepala chosiliza chikwati nakumupisha mukazi?" 8 Anayanka kuti, "Chifukwa cha kulimba mutima kwanu, ndiye chamene Mose anakuvomelezani kuti musiye bakazi banu, koma kuchokela pachiyambi sichinali njila iyi. 9 Nikuuzani imwe, ali onse wamene asiya mukazi wake, kuchoselako chifukwa cha uchiwelewele, ayenda akwatila na mukazi winangu, achita chigololo; nauja mwamuna wamene akwatila uja mukazi osiyiwa achita chigololo." 10 Bopunzila banamuuza Yesu kuti, "Kansi ngati ndiye mwamene chilili pali mwamuna na mukazi wake, sichintu chabwino kukwatila." 11 Koma Yesu anabayanka kuti, "Sibonse bantu bamene bangavomele chipunziso ichi, koma baja bamene bavomelesewa kuti bachivomele. 12 Chifukwa kuli baja bamene sibafuna chikwatila kuchokela kubadwa kwabo, futi kuli baja bamene sibafuna chikwatila chifukwa cha malamulo yabantu, nafuti kuli baja bamene sibafuna chikwatila chifukwa cha ufumu wa kumwamba. Wamene akwanisa kuchilandila ichi chipunziso, mulekeni achilandile. 13 Banaleta bana bangóno kuti aba ikepo kwanja nakuba pempelela, koma bopunzila bake banabakalipila. 14 Koma Yesu anabauza kuti, "Bavomeleseni bana bangóno, osabalesa kuti babwele kuli ine, chifukwa ufumu wakumwamba niwa bantu monga aba." 15 Anaika manja yake pali bana baja, nakuyenda kuchoka kumalo kuja. 16 Onani, muntu anabwela kuli Yesu nakukamba kuti, "Apunzisi, nichintu chiti chabwino chamene ine nifunikila kuchita kuti nipasiwe moyo wamene siusila?" 17 Yesu anamuyanka kuti, "Nanga nichani kansi chamene iwe unifunsila kuti chabwino nichiti? Pali chabe umozi wabwino, koma ngati ufuna kuti ungene mumoyo, sunga malamulo." 18 Muntu uja anayanka kuti, "Yati malamulo?" Yesu anayanka kuti, "Osapaye, usachita chigololo, usabe, usankale kamboni waboza, 19 lemekeza batate bako na bamai bako, ukonde muzako monga mwamene uzikondela iwe weka." 20 Uja mwamuna anamuyanka kuti, "Vonse ine nimachita. Nanga kwasala chani chamene nifunika kuchita?" 21 Yesu anamuyanka kuti, "Ngati ufuna kuti unkale ofikapo, yenda, kagulise vonse vamene ulinavo, upase bosauka, ndipo uzankala na chuma kumwamba; ubwele, unikonke." 22 Koma pamene munyamata uyu anamvela vamene Yesu anamuuza, anaenda omvesana chifundo, chifukwa anali olemela maningi. 23 Yesu anauza bopnzila bake kuti, "Zoona nikuuzani imwe, nichintu chovuta kuti muntu olemela angene mu ufumu wakumwamba. 24 Nafuti nikuuzani kuti, nichintu chapafupi kuti Kavalo ingene muka muboó ka nyeleti kuchila kuti muntu olemela angene mu ufumu wa Mulungu." 25 Pamene bopunzila bake banamvela ichi, banali banadabwa kwambili nakukamba kuti, "Kansi nanga nindani wamene angapulumusiwe?" 26 Yesu anabalangana nakukamba kuti, "Kuli bantu ichi nichintu chamene sichingakwanilisike, koma kuli Mulungu vintu vonse vikwanilisika." 27 Pamene apo Petulo anayanka kuti, "Onani, tinasiya vintu vonse naku kukonkani. Nanga ise tizapezamo chani?" 28 Yesu anabauza kuti, "Zoona nikuuzani imwe, mu mubadwe pamene Mwana wa Muntu azakankala pa mupando wake waulemelelo, naimwe bamene munanikonka muzakankala pa mipando zachifumu zili 12, kuweluza mitundu kumi na zibili zaku Israeli. 29 Ali wonse wamene anasiya manyumba, ba bale, balongo, batate bake, bamai bake, bana, kapena munda chifukwa cha zina yanga azakalandila kupitililapo ntawi zili 100 na kulandila moyo wamene siusila. 30 Koma bambili wamene bali boyambilila bazankala bosilizila, na baja bosilizila bazankala boyambilila.