Mutu 16

1 Ba Falisi naba Saduki banabwela kumuyesa eve kumufunsa kuti abalangise cholangiza chokokela kumwamba. 2 Koma anabayanka nakubauza kuti, "Pamene ikali ntawi yaku mazulo, mumakamba kuti, 'Kuzankala bwino lelo, chifukwa makumbi yaoneka monga ma magazi.' 3 Pamene kukucha, mumakamba kuti, 'lelo kzankala mpepo, chifukwa makumbi yaoneka monga magazi nafuti yavala kumwamba.'Imwe muziba tantauzo ya kaonekedwe ka makumbi, koma mukangiwa kuziba voonesa ntawi. 4 Mubadwe woipa wa chigololo ifunisisa choonesa, koma kulibe choonesa chamene chizapasiwa koma cha Yonah cheka." Pamene apo Yesu anabasiya naku enda. 5 Pamene bopunzila banafika kumbali ina, banaibala kunyamula buledi. 6 Yesu anabauza kuti, "Nkalani bochenjela ku votupisa vaba Falisi na ba Saduki." 7 Bopunzila banayamba kukambisana pakati pabo kuti, "Nichifukwa chakuti sitinanyamule buledi." 8 Yesu anaziba kuganiza kwabo nakubauza kuti, "Imwe ba chikulupililo chingóno, nanga nichani mukambisana pamweka kuti nichifukwa chakuti simunanyamule buledi? 9 Nishi simuona kapena kukumbuka ma buledi yaja yanali 5 ya bantu banali 5000, na mabasiketi yamene munatengelamo vinasala? 10 Kapena ma buledi yanali 7 ya bantu banali 4000, na mabasiketi yamene yanasalapo yamene munatenga? 11 Nanga nibwanji imwee simuona kuti sininali kukamba naimwe pali buledi? Nkalani wochenjela na votupisa vaba Falisi naba Saduki." 12 Pamene apa banaziba kuti sanali kubauza kuti basachenjele chifukwa cha chotupisa cha buledi, koma kuti bankale wochenjela chifukwa cha vipunziso vaba Falisi naba Saduki. 13 Pamene Yesu anabwela kumalo pafupi na Sizaliya na Filipi, anabafunsa bopunzila bake kuti, "Nanga bantu kansi bakamba kuti Mwana wa Muntu nindani?" 14 Banamuyanka kuti, "Benangu bakamba kuti ndiwe Yohane Mubatizi; benangu bakamba kuti Eliya; na benangu, Yelemiya, kapena umozi opunzila wa baneneli." 15 Anabauza kuti, "Nanga imwe mukamba ine ndine ndani?" 16 Mukuyanka, Simoni Petulo anakamba kuti, "Ndimwe Kristu, Mwana wa Mulungu wa moyo." 17 Yesu anayanka naku muuza kuti, "Ndiwe odalisika, Simoni mwana wa Yonah, chifukwa tupi na magazi sivamene vakuzibisa ichi, koma ba Tate banga bamene bali kumwamba. 18 Nikuuza futi kuti iwe ndiwe Petulo, pa mwala wamene uyu ine nizamanga kachisi yanga. Viseko vaku Hadesi sivizakwanisa kupambana. 19 Nizakupasa mfungulo yaku ufumu wa kumwamba. Chilichonse chamene uzamanga pa ziko ya pansi chizamangiwa kuziko yaku mwamba, na chili chonse chamene uzamangusula paziko yapansi chimangusuliwa kumwamba." 20 Yesu anauza bopunzila bake kuti basauzeko muntu aliwonse kuti eve ni Kristu. 21 Kochokela ntawi yamene iyo Yesu anayamba kuuza wopunzila bake kuti eve afunika kuyenda ku Yelusalemu, akavutikisiwe mu vintu vambili mumanja yaba kulubakulu na bakulu ba nsembe na bolemba, akapaiwe, koma akauke kubakufa pa siku ya chitatu. 22 Petulo anamutenga kumbali Yesu naku mukalipila, kukamba kuti, "Ichi chinkale kutali naimwe, Ambuye; osati ivi vikakuchitikileni imwe." 23 Koma Yesu anapindamuka nakuuza Petulo kuti, "Yenda kumbuyo kwanga ine, Satana! Ndiwe chogwesa ine, chifukwa susamalila vintu va Mulungu, koma chabe va bantu." 24 Yesu anakamba kuli bopunzila bake kuti, "Ngati muntu aliwonse afuna kunikonka ine, ayenela kuzikana eka, anyamule mutanda wake, anikonke. 25 Chifukwa aliwonse wamene afuna kupulumusa moyo wake azautaya, na uja wamene ataya moyo wake chifukwa cha ine azaupeza. 26 Nanga pindu ilipati ngati muntu atenga ziko yonse koma ataya moyo wake? Nichichani chamene muntu angapase kuchinjanisa na moyo wake? 27 Chifukwa Mwana wa Muntu azakabwela mu ulemelelo waba Tate bake pamozi nabangelo bake. Kuchoka apa azakapasa muntu aliwonse malipilo kulingana navamene anachita. 28 Zoona nikuuzani imwe, pali benangu bamene bali imilile pano bamene sibazakaona imfa mpaka bakaone Mwana wa Muntu mu ufumu wake."