Mutu 17

1 Ma siku yokumana yali sikisi Yesu anatenga Petulo, Yakobo, na Yohane mubale wake, nakukwela nabo pamwamba pa lupili pa beka. 2 Anachinjisiwa pamenso pabo. Pa menso pake pabala monga zuba, na vovala vake vinankala vobala monga nyali. 3 Onani, banaonekela kuli beve Mose na Eliya ndishi bakamba na eve. 4 Petulo anavula kamwa nakukamkba kuli Yesu kuti, "Ambuye, nichabwino kuti ise kupeza pano. Ngati mufuna, nizapanga pano tu mitenge tutatu-kamozi kani, kamozi ka Mose na kenangu ka Eliya." 5 Pamene eve anali kukamba, onani, kumbi inaba vundikila, ndipo onani, munachoka mau mu kumbi, yokamba kuti, "Uyu ndiye Mwana wanga Wokondewa, wamene ine nimvela bwino. Mumveleleni." 6 Pamene bopunzila banamvela ivi, banagwada pansi namanta. 7 Yesu anabwela abagwila na kwanja nakukamba kuti, "Imani musachita manta." 8 Pamene apo banalanga kumwamba koma sibanaone ali onse koma Yesu eka chabe. 9 Pamene banali kubwelela kuchoka pa lupili, Yesu anabauza, kuti, "Musa uzeko muntu ai onse pali ivi vamene mwaona koma pamene Mwana wa Muntu azaka ukishiwa ku bakufa." 10 Bopunzila bake banamufunsa, kuti, "Nanga nichani bolemba bama kamba kuti Eliya ndiye wamene ayenela kuyambilila kubwela?" 11 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Eeeh Eliyah ndiye wamene azayambilila kubwela kukonza vintu vonse. 12 Koma nikuuzani imwe kuti, Eliya anabwela kudala, koma sibanamuzibe. Koma, banamuchitila vonse vamene banali kufuna kuli eve. Chimozi-mozi, Mwana wa Muntu azakavutika mumanja yabo." 13 Pamene apo bopunzila bake banaziba kuti anali kuba uza pali Yohane Obatiza. 14 Pamene banabwela kumene kunali gulu yabantu, mwamuna umozi anabwela kuli eve, anagwada pansi, naku kamba kuti, 15 "Ambuye, chitilanikoni chifundo mwana wanga, chifukwa adwala makate ndipo amavutika maningi. Kambili amagwela pa mulilo penangu mumanzi. 16 Nenze namu leta kuli bopunzila banu, koma bakangiwa kumupolesa." 17 Yesu anamuyanka, "Bosakulupilila mubadwe oĆ³nongeka, kansi ninkale naimwe ntawi itali bwanji? Kansi ninkale ozigwila ntawi itali bwanji? Muleteni kuno kuli ine." 18 Yesu anachikalipila chija chi muzimu, chinachoka nochoka muli eve chija chimuzimu, na uja mwana anapola ntawi yamene ija. 19 Bopunzila banabwela kuli Yesu pa beka nakukamba kuti, "Nanga nichani chamene ise takangiwila kuchichosa?" 20 Yesu anayanka kuti, "Chifukwa ndimwe bochepa chikulupililo. Niku-uzani kuti, ngati muli nacho chikulupililo olo chochepa monga ka mbeu kampilu, munga chi uze ichi chi lupili kuti, 'Choka apa uyende paja,' ndipo chizafendela, kuli chamene chizankala choshupa kuli imwe." Ma buku yenangu yakudala maningi yalibe ndime ya 21 21 "Koma ivi va mutundu uyu sivima choka koma ngati mwazimana chakudya na pempelo." 22 Pamene bakanali mu muzinda wa Galileya, Yesu anauza bopunzila bake kuti, "Mwana wa Muntu aza pelekewa mumanja ya bantu, 23 ndipo bazamupaya, koma pa siku ya chitatu azakaukishiwa kubakufa." Bopunzila bake banankala bokalipa. 24 Pamene banafika mu muzinda wa Kapenamu, bantu baja bamene banali kutenga ndalama za mu tempele banabwela kuli Petrosi nakumuuza kuti, "Nanga bapunzisi banu bamalipila musonko wamu tempele?" 25 Anabayanka kuti, "eeeh." Pamene Petrosi anabwela munyumba, Yesu anamufunsa kuti, "Nanga iwe uganizapo bwanji, Simoni? Nanga nikuli bandani kwamene mfumu za pa ziko zima tengako musonko kapena volipilisa? Kuli bana babo kapena bantu benangu chabe?" 26 "Kuli bantu benangu chabe," Petulo anabayanka. Kansi ndishi bana nibomasuka," Yesu anamuyanka. 27 Koma kuti ise tisa lengese bantu bamusonko kuti bachimwe, enda ku nyanje, uponye musozo, utenge nsomba yamene izayambilila gwiliwa. Uivule kamwa, uzapezamo ndalama. Itenge uyende ukapase bamusonko kulipilila iwe na ine."