Mutu 15

1 Ba Falisi naba Bolemba banabwela kuli Yesu kuchokela ku Yelusalemu. Banakamba kuti, 2 "Nanga nichani bopunzila bako sibakonka myambo za makolo? Chifukwa sibasamba kumanja pakudya." 3 Anabayanka kuti, "Nanga naimwe nichani chamene mupwanyila lamulo ya Mulungu chifukwa cha myambo zanu? 4 Chifukwa Mulungu anakamba kuti, 'Lemekeza batate bako na bamai bak', nafuti kuti 'Eve wamene anyoza ba tate bake kapena bamai bake azapaiwa.' 5 Koma imwe mukamba kuti, 'Ali onse wamene auza tate wake kapena mai wake kuti, "Tandizo ili yonse yamene imwe munalandila kochokela kuli ine ni mpaso yopelekewa kuli Mulungu," 6 wamene uja muntu futi safunikila kulemekeza batate bake.' Chifukwa cha ichi mwalengesa kuti mau ya Mulungu yankala yalibe mpavu chifukwa cha myambo zanu. 7 Imwe bantu baboza! Zoona mwamene Yesaya ananenela pali imwe pamene anakamba kuti, 8 'Aba bantu banilemekeza chabe pakamwa, koma mitima zabo zili kutali na ine. 9 Bapembeza ine mwachabe chifukwa bapunzisa kunkala vipunziso malamulo ya bantu.'" 10 Anabwela aitana gulu kuti ibwele kuli eve naku iuza kuti, "Mvelani nafuti mumvesese- 11 Kulibe chintu chamene chingena mukamwa naku lakwisa muntu uyo. Koma, chamene chichoka mukamwa, ndiye chamene chima lakwisa muntu. 12 Bopunzila banabwela naku mu-uza Yesu kuti, "Nanga muziba kuti ba Falisi bamakalipa bakamvela mau aya?" 13 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Mutengo uli onse wamene ba Tate banga sibana shange uzanyuliwa. 14 Basiyeni beka, nibasogoleli balibe menso. Ngati mpofu asogolela mpofu winangu, bonse bazagwela mumugodi." 15 Yesu anayanka nakukamba kuti, "Tiuzeni chikambidwe ichi." 16 Yesu anayanka kuti, "Naimwe monse simuziba kukamba uku? 17 Nanga simumaona kuti chintu chilichonse chamene chingena mukamwa chima enda mumala naku choka kuyenda muchimbuzi? 18 Koma vintu vamene vamachoka mukamwa vimachokela mumutima. Ivi ndiye vintu vamene viononga muntu. 19 Chifukwa mumutima wa muntu ndiye mwamene mumachokela maganizo yoipa, kupaya, vigololo, uchiwelewele, ukawalala, ukamboni waboza, na kunyozela. 20 Ivi ndiye vintu vamene vima ononga muntu. Koma kudya pamene sunasambe kumanja sikumaononga muntu. 21 Pamene apo Yesu anenda kuchoka kuja kumalo naku yenda kumalo yaku dela yaku Taya naku Sidoni. 22 Onani, muzimai waku Kanani anabwela kuchoekela kumalo yaja. Anapunda naku kamba kuti, "Nimvelelenikoni chifundo ine, Ambuye, Mwana wa Davide! Mwana wanga mukazi atengewa maningi nachibanda." 23 Koma Yesu sanamuyanke mau yali yonse muzimai uyu. Bopunzila bake banabwela nakumupapatila kukamba kuti, "Mupisheni uyu aende, chifukwa atipundila ise." 24 Koma Yesu anayanka naku kamba kuti, "Ine sininatumiwe ku muntu ali onse koma chabe kuli nkosa za munyumba ya Izilayeli." 25 Koma anabwela naku gwada pamenso pake, nakukamba kuti, Ämbuye, nitandizeni ine." 26 Anamuyanka naku kamba kuti, "Sichintu chabwino kutenga buledi yabana naku itaila kuli tu imbwa tubana." 27 Anakamba kuti, "Zo-ona, Ambuye, koma na tu imbwa tungóno tumadya votaikila kuchoka podyela bene bake." 28 Pamene apo Yesu anayanka nakumuuza eve kuti, "Muzimai, uli na chikulupililo chikulu; leka chikuchitikile monga mwamene iwe ufunila." Pamene apo mwana wake mukazi uja anapola. 29 Yesu anachokako kumalo kuja naku yenda ku nyanja yaku Galileya. Anaenda akwela pa lupili naku nkala pamene paja. 30 Magulu yabantu yanamukonka. Banamuletela bantu bolemala, mpofu, bachi ulu, na bantu bopunduka, na baja bamene banali bodwala. Banabaika pafupi na Yesu, anabapolesa. 31 Gulu ija inadabwa kwambili pamene banaona bachi ulu bayamba kukamba, bopunduka bapola, bolemala bayenda, na mpofu ziona. Banatamanda Mulungu waku Izilayeli. 32 Yesu anaitana bopunzila bake nakubauza kuti, "ine gulu ya bantu yanimvesa chifundo chifukwa chakuti bankala naine masiku yatatu pamene apa koma balibe na vakudya. Sinifuna kuba pisha bakalibe kudya kali konse, chifukwa banga komoke munjila." 33 Bopunzila banamuuza kuti, "Manje nanga nikuti kwamene tingagule mukate wamene ungakwanile kudyesa gulu ikulu iyi ya bantu kuno kumalo kwamene sikunkala na bantu?" 34 Yesu anabayanka kuti, "Nanga ma buledi yamene muli nayo niya ngati? Bana yanka kuti, "Yali seveni, na tu nsomba tungóno." 35 Yesu anabauza gulu ija kuti inkale pansi." 36 Anatenga ma buledi yali seven yaja na nsomba, pamene ana yamika, ana suna ma buledi yaja naku yapasa kuli bopunzila bake. Bopunzila bake bana gabisa gulu. 37 Bantu bonse banadya naku kuta. Bana tenga ma buledi yanasalako muma basketi. 38 Baja bamene banadya banali four sauzande bamuna, kosapendelako bazikazi na bana. 39 Kuchoka apa Yesu anapisha yaja magulu kuti yayende pamene apo anakwela mu bwao naku yenda ku malo yaku Magadana.