Mutu 3

1 Onani chikondi camene Atate anatipasa ife, kuti tiitanidwe ana a Mulungu, ici ndi mwamene tilili. Pa chifukwa ici, dziko lapatsi siitiziba, chifukwa siinamuzibe iye. 2 Wokondedwa, manje ndife bana ba Mulungu, ndipo cenze cikalimbe kuonesewa mwamene cizankhalila. Tiziba kuti pamene kristu azaonekela, tizankala ngati iye, chifukwa tizamuona mwemene alili. 3 Aliwonse alina chisimikizo cazakusogolo aika nzelu zake mwaiye ndipo aziiyelesa mwamene iye ali woyela. 4 Aliwonse wamene apitiliza kucimwa achita vosa vomelekezedwa, cimo nicosa vomelekezedwa. 5 Muziba kuti Kristu anaonesedwa kuti achose cimo. Ndipo mwa iye mulibe cimo. 6 Kulibe amene akhala mwa iye apitiliza kucimwa, kulibe amene apitiliza kuchimwa anamuona kapena kumuziba iye. 7 Bana anga okondedwa, musalole aliwose akusobeseni. wamene achita chilungamo niolungama. 8 Monga Kristu niolungama.Amene acita cimo ni wasatana, Chifukwa satana anacimwa kuchoka pachiyambi. Pa chifukwa ici mwana wa Mulungu anaonesedwa, kuti aononge nchito ya satana 9 Aliwonse anabadwa mwa Mulungu samachimwa chifukwa mbeu ya Mulungu inkhalilila mwa iye Sangapitilize kuchimwa chifukwa anabadwa kufumila mwa Mulungu. 10 Mwaichi bana ba Mulungu ndi ana ba satana ba onekela. Aliyense wamene sachita chilungamo sachokela kwa Mulungu, ngakale iye amene sakonde mbale wake. 11 Uyu ndiye uthenga wamene munavela kufumila pachiyambi: kuti tizikondana wina ndi muzake, 12 osati monga Kaini, amene anacoka kuwoyipa napaya mubale wake. Nanga anamu paila chani? chifukwa nchito zake zinali zoyipa, ndipo mbale wake zinali zachilungamo. 13 Osankhala wodabwa, abale anga, ngati ziko ikuzondani. 14 Tiziba kuti tinapita kucoka ku ifa ndikuyenda kumoyo, chifukwa tikonda abale athu. 15 Aliyense wamene sakonda akhalila muimfa. Aliyese wamene azonda mbala wake niwakupha. Ndipo muziba ati umoyo wosatha siwu nkhala mu munthu wakupha. 16 Mwaichi tiziba chikondi, chifukwa Kristu anataya moyo wake chifukwa ca ise.naise tifunika kutaya moyo wake chifukwa cha abale athu. 17 koma aliyese ali na kathundu wamuziko, naona mbale wake akufuna nakuvala mutima wake wachifundo kwayeve, Nanga chikondi cha Mulungu chinkhala bwaji mwa iye? 18 Bana banga okondedwa, tisakonde ndi mau cabe kapena ndililime cabe, koma mukucita ndi mchoonadi. 19 Ndi mwaici mwamene tiziba kuti tinachokela kuchoonadi, ndipo tisimikiza mitima yasu pamenso pake. 20 Ngati mitima yathu itisusa, Mulungu nimukulu kupambana mitima yathu, Ndipo aziba zithu zonse. 21 Wokondedwa, ngati mitima yathu siitisusa, tili ndi chisimikizo kwa Mulungu. 22 Chilichonse camene timpempa tiza landila kuchokela kwa iye, chifukwa tisunga malamulo ndipo tichita zamene zimukondwelesa iye. 23 iyi ndiye lamulo lake: Kuti tikulupilile muzina ya mwana wake Yesu Kristu ndi kukondana wina ndi muzake, monga mwamene anati phasila malamulo aya. 24 Amene asunga malamulo a Mulungu ankhalilila mwa iye, ndipo Mulungu ankhalilila mwa iye. Mwaichi tiziba kuti akhalilila mwaise, mwa Muzimu wamene iye anatipasa.