MUTU 2

1 Imwe bana bango'no, nikulembelani izi zinthu kuti musachimwe.koma ngati wina achimwa, tilinaye otipapatila ndi atata, Yesu Kristhu wamene ali oyela. 2 Ni muombolo wama chimo yatu, Ndiponso siise teka, Ndiponso wa ziko lonse. 3 Paliichi tiziba kuti timuziba:ngati tasunga malamulo yake. 4 Wamene akamba, ''Ati ni muziba Mulungu,'' koma siasunga malamulo yake,ni waboza, na choonadi sichi muli iye. 5 koma wamene asunga mau yake,choonadi, ndiye wamane batate ba konda ndi choonadi chake ni chosilizika. paliichi tiziba kuti, timuziba. 6 Wamene akamba kuti azankalili muli iye, afunikila kuyenda monga mwame Yesu Kristhu anaendela. 7 Okondedwa, sinikulembela malamulo ya sopano kuli iwe, koma niya kudala yamene munali nayo pachiyambi. malamulo yakudala ndiye mau unamvela. 8 komanso ni kulembela malamulo yasopano kuli iwe, ndiye ya choonadi muli kristhu, chifukwa mfinzi ilikupita, ndi nyali yachendi ilikuwala kudala. 9 Iye wamene anena kuti ali munyali koma azonda mubale wake akali munfinzi namanje. 10 wamene akonda mubale wake ankalilila mu nyali ndiponso kulibe chamene chingamulenge kuzibuntula. 11 koma wamene azonda mubale wake alimunfinzi ndiponso akalikuyendela munfinzi; ziazi kwamene ayenda, chifukwa nfinzi yaboola menso yake. 12 Nilembela imwe, bana, chifukwa machimo yanu yakululukidwa chifukwa chazina yake. Nilembela kwainu azitate, chifukwa muziba wamene ili kuchiyambi. 13 Nilembela inu amuna achichepele, chifukwa muna gonjesa woyipa. 14 Nalembela kwainu atate, chifukwa mumuziba uja wamene anali kuchiyambi. Nalembela kwainu amuna achichepele, chifukwa ndimwe olimba, ndipo mau ya Mulungu yankalilila mwa imwe. ndiponso mwagonjesa uja woyipa. 15 Musakonde ziko angankale zinthu zamenezili muziko. ngati wina wache akonda ziko, ndi chikondi chaatate sichili muli iye. 16 chifukwa zonse zamene zili muziko__kukumbwila paza muthupi, kukumbwila kwa menso,ndi ntota zaumoyo__siwakuli atate koma niwa kuziko. 17 ziko ndizo lakalaka zache zili kupita. koma alionse wamene achita chifunilo cha Mulungu azankalilila muyayaya. 18 Imwe bana bango'no, iyi ni ntawi yosilizila, monga mwamene munamvelela kuti bambili bosusana kristhu babwela.paichi tiziba kuti ni ntawi yosilizila. 19 Banachokela kuliise , koma sibana chokele mwaise. chifukwa ngati banalikuchokela mwaise, asembe anankhalilila mwaise. koma pamene banaenda, sibalangiza kuchokela kuliise. 20 Koma mulina muzozo kuchokela kuli oyela.ndiponso bonse muziba choonadi. 21 sininalembele kwa imwe chifukwa simunazibe choonadi, koma chifukwa muchiziba ichi ndiponso chifukwa kulibe boza yamene ichokela mu choonadi. 22 Ni ndani waboza koma uja wamene akana Yesu kuti ni Kristhu? uja muntthu ni osusana kristhu, chifukwa akana atate ndi mwana. 23 kulibe wamene aka mwana angankale na tate.Alionse wamene azindikila mwana ndiiyenso alinatate. 24 koma kwaimwe,siyani vamene munasiya kuchiyambi visale muli imwe.ngati vamene munamvela kuchiyambi vasalila mwaimwe, ndiponso muzankhalilila mu mwana ndi atate. 25 Iyi ndiye lonjezo anatipasila: moyo wamuyayaya. 26 Nalemba izi zinthu kamba kabamene bangakukusobeseni. 27 Koma kwaiwe, muzozo wamene unalandila kuchoka kuli iye unkhalilile, ndiponso siufunika wina kukupunzisa. koma mwamene muzozo wake umapunzisila imwe zonse ndiponso ni wachoonadi siwaboza,monga mwamene anakuuzilani nkhalililani muli emve. 28 Manje,imwe bana, nkhalililani muli iye, pakuti akaonekela, tizankhala olimba muthima ndiponso sitizamvesewa manyazi pakubwela kwake. 29 Ngati muziba kuti niolungama, muziba kuti ali onse wamene amachita cholungama niobadwa kuchokela kwaiye.