Mutu 4

1 Ha, ndiwe okongola, okondewa wanga; ndiwe okongola. Menso yako yali kwati nkunda kuseli kwa chovinikila chako. Sisi yako ili kwati gulu ya mbuzi yo chokira ku phili ya Giliyadi. 2 Meno yako yali kwati gulu ya nkhosa zikazi zongometa kumene, zobwera kuchokela kumalo osambilako. Aliyense ali na mapasa, ndipo palibe aliyense mwa iwo amene wafeledwa. 3 Milomo yanu ili kwati ulusi wofila kwambili; mukamwa mwako ndiwe okongola. Masaya yako yali kwati makangaza ya makangaza kuseli kwa chophimba chako. 4 Mukosi wako uli kwati po yanganila anamanga Davide mumalile ya myala, na zikwi na vishango zishango pokolobeka, zonse zishango za bakondo. 5 Mabele yako yali kwati bana ba bili yamapasa insa, kudya musipu pakati pa maluba. 6 Mpaka mbandakucha na mutunzi kusana tabe, nizayenda phili ya myrra na kuchulu cha lubani. 7 Ndiwe okongola munjila zonse, okondewa wanga ndipo palibe choipa pali iwe. 8 bwela naine kuchoka mu Lebanoni, mukwatibwi wanga. Bwelani naine ku choka ku Lebanoni; choka pa mwamba pa Amana, pamwamba pa Senili na Hermoni, mumapanga ya nkalamu, kuchoka muma pili ya mapanga ya kaingu. 9 Waba mutima wanga, mulongo wanga, mukwatibwi wanga; mwaba mutima wanga, pakuni langana chabe kamozi, na mwala umozi wa mumukosi wako. 10 Nicha bwino bwanji chikondi chako, mulongo wanga, mukwatibwi wanga! Nanga chikondi chako chipitilila vinyo bwanji, naku nunkila kwama futa yako monga vonunkililisa vosiyana siyana. 11 Milomo zako, mukwatibwi wanga, yachosa uchi; uchi na mukaka vili pansi pa lilime yako; ku nunkila kwa chovala chako kuli monga ku nunkila kwa Lebanoni. 12 Mulongo wanga, mukwatibwi wanga ni munda ovaliwa, munda ovaliwa, kasupe yo vinikilika. 13 Misambo zako ni zomela za mutengo wa makangaza na zipaso zabwino kwambili, na zipaso za henna naza nado, 14 nado na safironi, Calamusi na Cinamoni namitengo zonse zo nunkilisa, Myrri na aloesi navonse vo nunkilisa vabwino. 15 Ndiwe kasupe wamu munda, chisime chamanzi yasopapano, misinje yoyenda kuchokela ku Lebanoni. 16 Nyamuka, mpepo yakumwela; bwela ,mpepo yakumpoto; fuzilila mumunda mwanga kuti zonunkila zake zichosa ku nunkhila kwake. Lekani okondewa wanga angene mu munda mwake na kudya vina mwavipaso vabwino.