Chapita 17

1 Iyi ndiye inali yabo ya malo ya mutundu wa manase (Amene anali mwana boyamba wa Yosefe) - yamene, niya makir, wamene anali mwana boyamba wa manase na wamene yeve anali tate wa Gileadi. Bana ba makir banapasiwa malo ya Gileadi na Bashani, cifukwa makir anli munthu wankhondo. 2 Malo yanapasiwa kul munthu bosala wa manase, kupasiwa kuli mabanja yabo - Abiezer, Kerek, Asriel, shechem, Hepher, na shemida. Aba banali bana bamuna ba manase mwana wa Yosefe, monga mwabanja yabo. 3 Manje, zelophehad mwana wa Hepher mwana wa Gileadi mwana wa makir mwana manase analibe bana bamuna koma bakazi cabe. Mazina yabana bakazi yanali mahlah, Noah, Hoglah, Milkah, na Tirzah. 4 Anabwela kuli Eliyaza wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, naba sogoleli, nakukamba kuti,'' Yehova analamulila Mose kutipasa coloba pamozi na babale banthu.'' Ndipo, kukonka cilamulo ca Yehova, anapasa azimai baja coloba pakati ka bale batate bake. 5 Magabo yali teni (10) yamalo yanapasiwa kuli manase mu Gileadi na Bashani, yamene ili ku mbali ina ya Yolodani, 6 Cifukwa bana bakazi ba manase banalandila coloba pamozi nabana bamuna. malo ya Gileadi yanapasiwa kuli bana bosala ba manase. 7 Malo ya manase yanafika kucoka pali Asha kufika ku mikmethath, yamene ili kumawa kwa shachem. Pamenepo malile yanayenda kubwela kuli baja bokhala pafupi na cisime ca Tappuah. 8 (Malo ya Tappuah yanali ya manase, koma muzinda wa Tappuah pa malile ya manase yanali ya banthu ba Eflemu). 9 Malile yanapita pansi kumusinje wa kanah. Aya mizinda yamisinje pakati pa mizinda ya manase yanali ya Eflemu. Malile ya manse yanali ku mpoto ya ku musinje, ndipo inasilila panyanja. 10 Malo yako mwela yanali ya eflemu, na malo ya ku mpoto yanali ya manase; nyanja inali malile. Kumbali ya ku mpoto angakumane na Asha na kumawa, Issachar. 11 Namuli Issacha na Asha, manase anatenga Beth shana mizi yabo, Ibleam na mizi yabo, bokhala mu Dor na mizi yake, bokhala bamu Fndor na mizi yabo, bokhala bamu Taanach na mizi yake, na bokhala baku megiddo namizi yabo (na muzinda wacitatu ni Napheth). 12 Koma mutundu wa manase sunatengeko mizinda yaja, popeza Akanani anapitiliza kukhala malo. 13 Pamene bantu ba Israyeli banakula mphavu, banaika ba kanani kupapa kwacika kamizo, koma sanabaco selemotu. 14 Pamenepo bana ba Yosefe anakamba kuli Yoswa, kuti,'' cifukwa cani watipa cabe yabo imozi ya malo na mbali imozi ya coloba, papeza ndife banthu bambili ngako, na kudala Yehova atidalisa?'' 15 Yoswa anakamba kuli beve,'' ngati ndimewe banthu bambili, yenda musanga nakukonza minda yanu mu malo ya Aperezi na ba Rephaim. Cipani ici popeza phili yaziko ya Eflemu niyai ng'ono kuli imwe. 16 Bana ba Ysefe banakamba kuti,'' phili ya ziko siyingakwanile ise. koma ba kanani bonse bamene banakhala mucigwa ali namagaleta ya nsimbi, bonse bamene bali mu Beth shani na mizi yabo, na baja bali mucigwa ca Jezreal.'' 17 Pamenepo Yoswa anakamba kunyuma ya Yoswa - kuli Eflemu na manase, '' ndimwe banthu bambili munambala, nakuti muli na mphavu zikulu. simufunika kukhala cabe na malo yamozi yokupasani. 18 Phili ya ziko izi khalanso yanu, nangu nisanga, muzalimapo nakutengo kufika kumalile yakutali. Muzacosamo Akanani ingakhale bali namagaleta ya nsimbi, nangu ni ba mphavu.''