Chapita 18

1 Ndipo musonkano bonse wa bana ba Israyeli banakumana pamozi pa shiloh. Banaika cihema cokumanilamo paja nakugonjesa malo pamenso pabo. 2 Panali mitundu ili seveni pakati kabana ba Israyeli bamene coloba cabo sicina gabwe. 3 Yoswa anakamba ku bana ba Israyeli kuti,'' mucebwa paka liti kungena mumalo yamene Yehova, mulungu wamakolo yanu, akupasani? 4 Zisankhileni bamuna batatu kucoka kumutundu ulibonse, ndipo nizabatuma. Bazayenda nakubona malo pamwamba napansi. Bazalembe mwamene bayabo nela mwa coloba cabo, nakubwelelanso kuli ine. 5 Bazaigaba magabo yali seveni. Yuda azasala mu malo yabo ku mwela, na nyumba ya Yosefe iza pitiliza mumalo ya mpoto. 6 Uzalemba malo muzigabo zili seveni na kuleta zolemba kuli ine. Nizacita muele yanu pamanso ya Yehova mulungu wanu. 7 Alevi alibe gabo pakati panu, popeza unsembe wa Yehova ndiye coloba cabo. Gadi, Rubeni, na mutundu bgabika lva manase evalandila coloba cabo, kupitilila Yolodani. Ndiye coloba camene Mose mutumiki wa Yehova anabapasa.'' 8 Ndipo bamuna bananyamuka nakuyenda, Yoswa analamulila baja banayenda kulemba maonekedwe yamalo, kukamba kuti,'' yendani kumwamba na pansi mu malo nakulemba mwamene yabonekela nakubwelela kuli ine. Nizacitila imwe maele pano pamene ya Yehova pa shiloh. 9 Bamuna banayenda nakuyenda - yenda pamwamba na Pansi mu malo na kulembe maonekedwe mubuku mwa mizinda yake muzigabo zili seveni, kulemba mizinda mucigabo ciliconse. pamenepo banabwelela kuli Yoswa mucigono ca shiloh. 10 Pamene Yoswa anabacitilako maele pashiloh pamenso ya Yehova. pansi paja kuti Yoswa anagabila malo bana ba Israyeli, kui alibonse anapasiwa gabo ya malo. 11 Kugaba kwa malo ya mutundu wa Benjamini banja pa banja. malile yamalo yabo yogabiwa yanali pakati pa bana ba Yuda bana ba Yosefe. 12 Kumbali yako mpoto, malile yabo yayambila pa Yolodani. malile yabo yanakwela kumumpoto kwa Yeliko, na kumwamba kupitilila muphili ya ziko kumazulo. kuja inafika mucipululu ca Beth Aven. 13 Kucokela kuja malile yanapitila ku mwela kunjila ya Lvz (malo yamozi monga Beteli) pamenepo malile ili kumwela kwa Beth Holoni. 14 Malile pamenepo yanayenda njila ina; kumbali ya kumazulo inakonekela ku mwela, kuyenda ku ma phili kusogolo kwa Beth Holoni. Aya malile yasilila pa kiriath baal (yamene, ni kiriath Jearim), muzinda unali wa mutundu wa Ayuda. Ici cinapanga malile ku mbali yaku mazulo. 15 Mbali ya ku mwela inayambila kunja kwa kiriath Jearim. Malile yanacokela kuja kuyenda ku Ephroni, ku cisime camanzi ya Nephtoah. 16 Malile pamenepo yanayenda pansi kumalile ya cigwa ca Rephaim. ndipo inayenda pansi ku cigwa ca Hinnom, kumwela koselukila kwa Ayebusi, na kupitilila pansi ku En Rogel. 17 Inakonekela kumpoto, kuyenda njira yaku En shemesh, nakucoka kuja inacoka kuyenda ku Geliloth, yamene inali pafupi na Adummim. pamenepo inayenda pansi ku mwala wa Bohan mwana wa Rubeni. 18 Inayendela kumu mpoto kwa Beth Araba na pansi ku Araba. 19 Malile yanayenda kumbali ya ku mpoto kwa Beth Hoglah. Malile yanasilila kumwela wa nyanja ya mucele, posilizila Yolodani kumwela. Aya ndiye yanali malile ku mwela. 20 Yolodani inapanga malile yake kumbali yakumawa. Ndiye cinali coloba ca mtundu wa Benjamini, ndipo cinapasiwa ku banja na banja, malilena malile, mo zungulila. 21 Manje mizinda yamitundu ya Benjamini, banja na banja, yanali na mizinda aya: Yeliko, Beth Hoglah, Emek kaziz, 22 Beth Arabah, Zemaraim, Beteli, 23 Avvim, Parah, Ophrah, 24 Kephar Ammoni, Ophni, na Geba, Tanali mizinda tyovv (12) kafakilako mizi yabo. 25 Kunalinso mizinda ya Gibeon, Ramah, Beeroth, 26 Mizpah, Kephirah, Mozah, 27 Rekem, Irpeel, Taralah, 28 Zelah, Haeleph, Jebus (cimozi mozi monga Yelusalemu), Gibeah, na Kiriath yanali mizinda fotini, kufakilako mizi yabo. Ndiye cinali coloba ca Benjamini ca mabanja yabo.