Chapita 13

1 Manje Yoswa anakalamba pamene Yehova anakamba kuli yeve,'' wakalamba, koma kukali malo yambili yafunika kutenga. 2 Aya ndiye malo yamene yakaliko: malile yonse ya Afilisti, nabonse ba Geshurites, 3 Kucoka ku shihor, kumawa kwa Eigipito, na kumpoto kwamalile ya Ekloni, ywmene itengewa monga katunda wa Akanani; Basogoleli bali faivi (5) ba Afilisti, baja baku Gaza, Ashdod, Ashkelo ni, Gath, na Ekroni - malo yaba Avvites. 4 Kuwela (malo ya Avvites); malo yonse ya Akanani, kucokela ku Arah yamene ipezeka ku sidonians, kutali kufika ku aphek yamene ili pamalile ya Amoni; 5 Malo ya ba Gebalites, Kulebanone konse kuyenda kumawa, kucoka ku Baal Gad pansi pa phili ya Hermon ko Lebo Hamath. 6 nakvikapo bonse bonkhala muphili yaziko kucoka ku Lebanoni kufika ku misrephoth maim, kuikako nabanthu bonse baku sidon. Nizacosa pamenso ya bankhaondo ba Israyeli . Onani kuti mupase malo kuli Israyeli monga yabo, mwamene ni nalamulila. 7 Gabani aya malo monga yanu yanu kumitundu yali naini (9) na mtundu bogabika wamanase.'' 8 Namutundu bogabika wina wamanase, A Rubeni, na ba Gadites banalandila malo yabo yamene Mose anabapasa kumbali yakumawa kwa Jolodani, 9 Kucokela Aroer, yamene ili mumbali mwa mumana wa Aroni (kuikako na muzinda uli pakati pa cigwa), naku cidikha conse ca medeba kufika ku Dibon; 10 Mizinda yonse yaku sihon, mfumu ya ba Amoni, analamulila mu Heshboni, kumalile ya Amoni, 11 Gileadi, na malile ya Geshurites na malile ya Geshurites na maacathites, na phili yonse ya Hermoni, na Bashan yonse ku salekah; 12 Naufumu bonse wa Og mu Bashani, amene analamulila mu Ashtaroth na Edrei - izi ndiye zina sula pali osala ba Rephaim - Mose anabakantha na kubacosa panja. 13 Koma banthu ba Israyeli sibanacose ba Geshurites kapena ba Maacathites. malo mwake, Geshur na maacath akhala pakati ka Israyeli lelo. 14 Kumutundu wa A Levi weka Mose sanapase coloba cao. zopeleka za Yehova, mulungu wa Israyeli, zopangiwa na muto, ndi coloba cabo, mwamene mulungu anakambila kuli Mose. 15 Mose anapasa coloba kumtundu wa A Rubeni, banja na banja. 16 Malo yabo yanali kuyambila ku Aroer, mumbali mwa mumana wa Arnoni, na muzinda uli pakati pacigwa, na cidikha conse ca medeba. 17 Rubeni naye analandila Heshbon na mizinda yonse yali mu cidika, Dibon, na Bamoth Baal, na Beth Baal meon, 18 na Jahaz, na kedemoth, na mephaath, 19 na kiriathaim, na sibmah, na zereth shahar pa phili ya cigwa. 20 Rubeni analandilanso beth peor, koselukila kwa pisgah Beth Jeshimoth, 21 Mizinda yonse ya ku cidikha, na ma ufumu yonse yaku sihon mfumu yaba Amoni, amene analamulila mu Heshboni, wamene Mose anagonjesa pamozi nabasogoleli ba midian, Evi Rekem, Zur, na Reba, kalonga wa sihon, amene anakhala mu ziko. 22 Bana ba Israyeli anapayafuti napanga Balaam mwana wa Beor, wamene anali kuombeza, pakati kabaja banapaya. 23 Malile ya mutundu wa Rubeni ni mumana wa Yolodani; ndiye malekezelo yabo. Ndiye cinali coloba ca Rubeni, kupasiwa kubanja iliyonse, namizinda zao na mizi zabo. 24 Ndiye vamene Mose anapasa kumutundu wa Gadi, banja na banja; 25 Malo yao yanali Hazer, mizinda yonse ya Gileadi na malo yoyabika ya Amoni, ku Aroer, yamene nikumawa kwa Rabbah, 26 Kucokela ku Heshbon kufika ku Ramath mizpah na Betonim, kucoka ku mahanaim kufika ku malile ya Debir. 27 Mucigwa, Mose anapasa Beth Haram, Beth Nimrah, succoth, na Zaphoni, na konse kwa ufumu wa sihon mfumu ya Heshboni, na Yolodani monga malile, kufika kosilizila kwa nyanja yaku kinnereth, kumawa kusogolo kwa Yolodani. 28 Ndiye coloba ca mtundu wa Gadi, banja na banja, namizinda yabo na mizi yabo. 29 Mose anapasa coloba ku mutundu bogabika wa manase. Inapasiwa kumutundu bogabika wa bana ba manase, banja na banja. 30 Malile yabo yanayambila ku mahanaim, na Bashani yonse, na ufumu bonse wa Og wa Bashani na mizinda yaku jair, yamene yali mu Bashani, mizinda sikisite; 31 Gileadi bogabika, na Ashtaroth na Edrei (mitundu ya ufumu yaku Og mu Bashani). Aya yanapasiwa kubana ba makir mwana wa manase - banthu bogabika pakati ba makir, banja na banja. 32 Ndiye colowa camene Mose anapasa kuli beve kumadimba ya moabu, kupitilila Yolodani kumawa kwa Yeliko. 33 Mose sanapase coloba kumutundu wa a Levi, Yehova, Mulungu wa Israyeli, ndiye coloba cabo, monga anakambila nabo.