Mutu 35

1 Ndipo Elihu anapitiriza kunena kuti, 2 "Kodi mukuganiza kuti ndi pamene mukunena kuti, 'Ndine wolungama pamaso pa Mulungu'? 3 ndipo, 'Kodi ndikadakhala bwino ndikadachimwa?' 4 Ndikukuyankha, iweyo ndi anzako. 5 Yang'anani kumwamba, muone; onani thambo, lomwe liri pamwamba kuposa inu. 6 Ngati mwachimwa, mumulakwira chiyani Mulungu? Ngati zolakwa zanu zaunjikana, mumatani naye? 7 Ngati ndinu olungama, mungamupatse chiyani? Adzalandira chiyani m'manja mwako? 8 Kuipa kwako kungapweteketse munthu, monga iwe ndiwe mwamuna, ndipo chilungamo chako chingapindulitsenso mwana wina wa munthu. 9 Chifukwa cha kuponderezana kochuluka, anthu amafuula; apempha thandizo m'manja mwa amuna amphamvu. 10 Koma palibe amene akuti, 'Ali kuti Mulungu Mlengi wanga, amene amatipatsa nyimbo usiku, 11 amene amatiphunzitsa zambiri kuposa momwe amaphunzitsira nyama zakutchire, ndi kutipanga ife anzeru kuposa mbalame za mlengalenga?' 12 Kumeneko amafuula, koma Mulungu samayankha chifukwa cha kunyada kwa anthu oyipa. 13 Mulungu samvera kulira kopusa; Wamphamvuyonse sadzalabadira za icho. 14 Nanga sangakuyankhani bwanji mukanena kuti simumuwona, mlandu wanu uli pamaso pake, ndipo mukumudikirira? 15 Tsopano mukuti mkwiyo wake sulanga, ndipo samazindikira ngakhale pang'ono za zolakwa. 16 Kotero Yobu amatsegula pakamwa pake kuti anene zopusa; amachulukitsa mawu osadziwa. "