Mutu 30

1 Pamene Recho anaona kuti sana mubalile bana Yakobo, Recho anakumbwila mulongosi wake. Anakamba kuli Yakobo kuti, "Nipase bana, olo inzafa." 2 Yakobo anakalipa chifukwa cha Recho. Anakmba kuti, "Ushe Ndine mulungu, anakulesa kuti unkale nabana?" 3 Anakamba kuti, "Ona, Pali wanchito wanga Bila. Gona naye, chakuti ati balile bana bolela pa mendo panga, ndipo ine nizankala na bana kupitila muli enve." 4 Chakuti anamupasa Bila wanchito wake kuti ankale mukazi wake, ndipo Yakobo aanagona naye. 5 Bila anankala na mimba nakubala mwana mwamuna wa Yakobo. 6 Pamene apo Recho anakamba kuti, "Mulungu anikambilako, ndipo anvela na mau yanga nakunipasa mwana mwamuna." Chifukwa chaichi anamuitana zina yake yake Dani. 7 Bila, wanchito wa Recho, anankala namimba futi naku balalila Yakobo mwana mwamuna wachibili. 8 Recho anakamba kuti, "Namenyana na mulongosi wanga mwampavu ndipo napambana." Anamuitana zina yake Nafutali. 9 Pamene Leya anaona kuti aleka kubala bana, anatenga Zelipa wanchito wake nakumupasa kuli Yakobo kuti ankale mukazi wake. 10 Zelipa, wanchito wa Leya, anabalila Yakobo mwana mwamuna. 11 Leya anakamba kuti, "Uyu ndiye mwayi!" chakuti anamuitana zina yake Gadi. 12 Pamene Zelipa, wanchito wa Leya, anabalila Yakobo mwana mwamuna wachibili. 13 Leya anakamba kuti, "Nakondwela! Chifukwa bana bakazi bazani itana ine kuti okondwela." Chakuti anamu itana zina yake Asha. 14 Rubeni anayenda mu munda pa masiku yochosa witi nakupeza maudeleki mu munda. Anayabwelesa kuli mayi wake Leya. Pamene Recho anakamba kuli Leya, "Unipaseko maudeleki yenangu ya mwana wako mwamuna." 15 Leya anakamba kuli enve, "Iyi ninkani ing'ono kuli iwe? kuti unanipoka mwamuna wanga? Manje ufuna kunitengela na mandeleki ya mwana mwanga mwamuna?" Recho anakamba kuti ndiye pamene azagona naiwe usiku walelo, chifukwa cha mandeleki yamwana wako yamene uzani pasako mochinjanisha." 16 Yakobo anabwela kuchokela kumunda mumazulo. Leya anayenda kukumana naye nakukamba kuti, "Ufunika kugona na ine, chifukwa nakugula na mandeleki." Chakuti Yakobo anagona na Leya usiku. 17 Mulungu anamunvelela Leya, anankala na mimba nakubalila Yakobo mwana mwamuna wa nambala faivi. 18 Leya anakamba kuti, "Mulungu anipasa ine malipilo yanga, chifukwa namupasa muzimai wanchito wanga kuli bamuna banga." Anamupasa zina yake Isaka. 19 Leya anankala namimba nakubala mwana mwamuna wa nambala sikisi wa Yakobo. 20 Leya anakamba kuti, "Mulungu anipasa ine mpaso yabwino. Apa manje mwamuna wanga azani lemekeza ine, ndaba namubalila bana bamuna bali sikisi." 21 Pasogolo pake anabala mwana mukazi nakumupasa zina yake Dinna. 22 Mulungu anakamba na Recho mumaganizo naku munvelela. 23 Anamulengesa kuti ankale na mimba. Anankala na mimba nakunkala na mwana mwamuna. Anakamba kuti "Mulungu anichosa nsoni zanga." 24 Anamuitana zina yake Yosefe, kukamba, kuti, "Yawe alundilapo kuli ine mwana mwamuna winangu." 25 Pasogolo pake Recho anabala Yosefe, "Yakobo anakamba kulli Labani "Munimasule, pakuti niyenfe kumunzi kwatu nako ziko yanga. 26 Munipase bakazi banga na bana banga bamene ninalipilila malipilo yokugwililani nchito, futi munileke niyende, kainge muziwa bwino nchito yamene nakugwili lani." 27 Labani anamu uza kuti, "Ngati apa uzani chitila chifundo mwamene uvionela vintu, uyembekeze, chifukwa nina ziba mumatesnga kuti Yawe anidalisa ine chifukwa cha iwe." 28 Pamene apo anakamba kuti, "kamba mutengo wako weka, ndipo ine nizabalipila." 29 Yakobo anakamba kuli enve, "Uziba mwamene ninatumikila kuli iwe, na mwamene vinyama vako vachitila twino kuli ine. 30 Pakuti mwenze natungo'no pamene ine nikalibe kubwela manje vapakilapo maningi. Yawe anakudalisani imwe paliponse peninali kusebenzela. Nanga niliti pamene nizapasako wamunyumba mwanga naine?" 31 Labani anafunsa kuti, "Nizakulipila chani?" Yakobo anakamba kuti "Simuzanilipila chilichonse. Ngati munga nichitele ichi chintu kuli ine, nizakavidyesa futi vinyama vanu nakusamala. 32 Lekani ine nipitemo pakati pa vinyama vanu lelo nakuchosapo ka shipi kalikonse kamene kali nama iwanga natuma dontho, ndipo kabulaki pa mbelele, ndipo katuma dontho namizele pagulu ya mbuzi. Aaya ndiye yazankala malipilo yanga. 33 Kukulupilika kwanga kuzakanikambilako pasogolo panga, mukayende kuona malipilo yanga. iliyonse yamene siyizankala na mizele na madoti pakati pa mbuzi, nayo kuda pakati pa mbelele, ngati iliyonse izakapezeka naine, izakaganizilidwa kuti niyakuba," 34 Laban anakamba kuti, "Anavomela. Leka mwamene wakambila mau yako." 35 Yamene ija siku Labani anachosapo mbuzi zimuna zamene zenzeli na mizele na madoti, na mbuzi zikazi zonse zamene zenze naka wayiti pa tupi, na zonse zokuda pakati pa mbelele, nakuzipasa mumanja mwa bana bake bamuna. 36 Labani anayikapo ulendo wamasiku yatatu pakati payenve mwine na Yakobo. Chakuti Yakobo anapititliza kusebenza kusunga vinyama va Labani vamene vina salapo. 37 Yakobo anatenga misambo yafuleshi yojubiwa yawisi ya mtengo wapopula, na mutengo wa alamondi, na mutengo wapuleni, naku fundulamo tumilayeni twa waiti mpaka va wayiti vamukati mwa chimutengo vinaonekela ku tumi tengo. 38 Pamene apo anayika tumitengo twamene anafundula pasogolo pa vinyama, pasogolo pama kontena yomweselamo manzi vinyama, pamene vinali kubwela kumwa manzi vinyama vinankala nama mimba pamene vinabwela kumwa manzi. 39 Vinyama vinali kugonana pafupi na tumitengo; ndipo vinyama vinabala bana bamizele, bamawanga na madoti. 40 Yakobo anapatulapo mutundu yuy wa tubana twa mbelele, koma analeka kuti zonse zinangu ziyangane ksayidi kwe kunali vinayama vamizela vo kuda pavinyama va Labani. Pasogolo pake anazichoselapo vinyama vake mwine yeka ndipo sanali kusankaniza pamozi na vinyama va Labani. 41 Paliponse nkosa zolimba muvinyana zikayamba kugonana. ninshi Yakobo analikugoneka tumitengo mumakontena yomwelesamo manzi vinyama, apo vinyama vilangana patumitengo. 42 Koma pamene vinyama vo foka maningi vinabwela, sanayike tumitengo pafupi navo. Chakuti vinyama vofoka vinankala va Labani, ndipo volimba vinankala va Yakobo. 43 Mwamuna yuy anankala olemela maningi. Anali na vinyama vambili, wanchito bakazi na bamuna, makameleo nama donke.