Mutu 28

1 Isaki anaitana Yakobo, anamu dalisa, nakumulamulila, "usaka tenge mukazi ochokela kuli bazikazi baku Kenani. 2 Nyamuka, yenda ku Padani Aramu, ku nyumba ya Bethueli ba mai ba batate bako naku tenga mukazi kuchoka kuja, umozi mwana mukazi wa Labani, mubale wa bamai bako. 3 Leka Mulungu wampamvu zonse aku dalise, aku pange obala ndipo akuchuluse kuti munkale bantu bambili. 4 Leka akupase daliso ya Abrahamu, kuli iwe, naku bana bobadwa pambuyo pako kuti ungene muziko yamene unali kunkalamo, yamene Mulungu anapasa Abrahamu." 5 Pamene apo Isaki anatuma Yakobo. Yakobo anayenda ku Padani Aramu, kuli Laban mwana mwamuna wa Betulo waku Aramea mubale wa Rebekah, ba mai ba Yakobo na Esau. 6 Manje Esau anaona kuti Isaki anadalisa Yakobo na kumutuma kuyenda ku Padani Aramu, kuti akatenge mukazi wa kuja. Anaona futi, kuti Isaaki anamudalisa na kumulamulila kuti, "usaka tenge mukazi pa bakazi baku Kenani." 7 Esau anaona futi Yakobo anamvelela batate bake naba mai bake, nakuyenda ku Padani Aramu. 8 Esau anaona kuti bakazi baku Kenani sibana kondwelese batate bake. 9 Pamene apo anayenda ku Ishmaeli, nakutenga, kumbali kwa bakazi bake, Mahalati mwana mukazi wa Ishmaeli, mwana mwamuna wa Abrahamu mulongosi wa Nebaioti, ankale mukazi wake. 10 Yakobo anachoka ku Beersheba naku yenda caku Harani. 11 Anabwela pa malo yena naku nkala kuja usiku onse, chifukwa zuba yenze inangena. Anatenga mwala umozi mu malo muja, naku ika pansi pa mutu wake, naku gona pa malo paja. 12 Analota naku ona makwelelo yana ima kuchoa pa ziko yapansi. Pamwamba pake panafika kumwamba ndipo bangelo ba Mulungu benzeli ku kwelapo naku selukapo. 13 Onani, Yehova anaimilila pamwamba pake naku kamba, "Ndine Yehova, MUlungu wa Isaki. Pa malo yamene ya gona nizapasa iwe na bana bobadwa muli iwe. 14 Bana bobadwa muli iwe bazankala monga doit yapansi, ndip muza zulana mutali wa kumazulo, kumawa, kumpoto, ndipo na kumwela,kupitlila muli iwe namuli bobadwila muli, mabanja yonse yapa ziko yaza dalisika. 15 Onani, Nili na iwe ndipo nizaku sunga kuli konse kwamene uzaka yenda. Nizakuleta iwe mu malo aya nafuti: chifukwa sisnizaka kusiya niza chita vonse vamene nina lonjeza kuli iwe." 16 Yakobo ana uka mutulo mwake, ndpo anakmba, "zo'ona Yehova ali pano pamalo, koma sininazibe. 17 Anali na manta naku kamba, "Niyo yoyofya bwanji aya malo! aya siyena koma nyummba ya Mulungu. Apa nipolobeka kumwamba." 18 Yakobo anauka kuseni maningi naku tenga mwala wamene anabwela afaka pasni pa mutu wake. Anachipanga nga chipilala naku tilapo mafuta pamwamba pake. 19 Anaitana zina malo yaja Betheli, koma zina ya muzinda uja inali Luzi. 20 Yakobo analapa chilapilo, kuti, "Ngati Mulungu azankala naine na kuni chigiliza pa njila iyi pamene niyenda, na kunipasa mukate okudya, na vovala vovala, 21 chakuti ine nibwelele mwamu tendele ku nyumba ya batate banga, pamene Yehova azankala Mulungu wanga. 22 Pamene mwala yuy wamene na imilika ngati pilala uzankala opatulika kuchokela pali vonse vamene wani pasa nizabwelesa chakumi kuli iwe."