Mutu 27

1 Pamene Isaki anakula na menso yake yanaleka kuonesesa kuti analeka nakuona, anaitana Esau, mwana wake mwamuna mukulu naku mu uza, "Mwana wanga." Esau anati kuli eve "Nili Pano," 2 ndipo Isaki anakamba, "Ona kuna nakota siniziba siku yamene nizafa. 3 Chifukwa chaicho tenga zida zako, chola chako cha mivwi, na uta wako, na kuyenda mu sanga nakunigwilila nyama. 4 Nipangile chakudya cha bwino, chamene nikonda, ndipo ulete kuli ine kuti nichidye na kuku dalisa iwe nikalibe kufa." 5 Ndipo Rabeka anamvela pamene Iski anali ku kamba na Esau mwana wake. Esu anayenda mu sanga kuti agwile nyama nakuleta. 6 Rabeka ana uza Yakobo mwana wake mwamuna kuti, "Yangana kuno, namvela atate bako bakamba na mubale waiko Esau. Bakamba kuti, 7 'Niletele nyama yamusanga ndipo unipangile chakudya chabwino, kuti nichidye naku kudatisa iwe pamenso ya Yehova nikalibe kufa.' 8 Ndipo chifukwa chaicho, mwana wanga, mvela mau yanga yamene niku lamula iwe. 9 Yenda kuvibeto nakuniletela tubana tw mbuzi tubili twa bwino; ndipo nizatupanga chakudya chabwino cha atate bako, monga mwamene bachikondela. 10 Uzapeleka kuli atate bako, kuti bachidye nakukudalisa bakalibe kufa." 11 Yakobo anauza Rabeka amai bake, " Onani, Esau mubale wanga ali na upipi, koma ine ndine mwamuna osalala, 12 kapena batate banga baza ni gwila ine, ndipo nizaoneka kuli beve ngati onama. Nizaziletela tembelelo neka osati daliso." 13 Amai bake bana mu uza eve, "Mwana wanga, leka tembelelo ibwele pali ine. Mvelela mau yanga, ndipo yenda, ulete kuli ine." 14 Ndipo Yakobo anaenda nakutenga tu bana twa mbuzi tubili naku tuleta kuli bamai bake, ndipo bamai bake bana panga chakudya chabwino, monga atate bake banali ku kondela. 15 Rabeka anatenga vovala va bwino va Esau, mwana wake mukulu mwamuna, wamene anali navo munyumba, naku valika Yakobo, mwana wake mungono mwamuna. 16 Ana muvalika chikumba cha ka mbuzi kangono ku manja yake na ku mbali yaku mukosi wake osalala. 17 Anaika chakudya cha bwino na mukate wamene anapanga mu manja mwa mwana wake mwamuna Yakobo. 18 Yakobo anaenda kuli ba tate bake naku kamba, "Batate banga." Batate bake bana kamba "Nili pano; ndiwe ndani mwana wanga?" 19 Yakobo ana bauza batate bake, "ndine Esau mwana wanu oyamba. Nachita monga mwenze mwani uzila. Manje ukani nakudyako nyama yanga yamusanga, kutimunidalisa ine." 20 Isaki ana mu uza mwana wake mwamuna, "Nanga wanga?" anati, "Chifukwa Yehova Mulungu wanu aileta kuli ine." 21 Isaki anati kuli Yakobo, "Bwela pafupi, pali ine kuti nikugwile iwe, mwana waga mwamuna, kuti nizibe gati zo ona ndiwe mwana wanga Esau olo kapena sindiwe." 22 Yakobo anayenda kuli Isaki tate wake, ndipo Isaki anamugwila naku kamba, "Mau ni mau ya Yakobo koma manja ni manja ya Esau. 23 Isaki sana muzibe, chifukwa manja yake yenze na upipi, monga ya mubale wake Esau, ndipo Isaki ana mudalisa. 24 Anakamba "Nanga ndiwe zo ona mwana wanga mwamuna Esau?" Anayanka, "Ndiwe" 25 Isaki anti "Leta chakudya kuli ine ndipo nizadya nyama yako yamu sanga, kuti nikudalisa." Yakobo ana muletela chakudya: Isaki anadya, Yakoba anamuletela vinyu, ndipo anamwa. 26 Ndipo atate bake ba isaki bana mu uza. "Manje bwela pafupi nakuni pyopyona mwan wanga mwamuna." 27 yakobo anabwela pafupi naku mupyopyona, ndipo ananusha kafungo ka vovala vake na kumudalisa anakamba "Ona, kafungo kam mwana wanga kali monga kamusanga mwamene Yehova ana dalisa. 28 Mulungu akapase mbali ya mame yako mwamba, mbali yakuina kwa ziko yapansi, na mbeu zambili na vinyu vanyowani. 29 Lekabantu baku sebenzele na maziko yakugwadile unkale bwana kuli ba bale bako, ndipo leka bana bamai bako bamuna baka gwadile iwe uyo wamene azaku tembelela atembelelewe: Wamene azakudalisa adalisiwe." 30 Pamene panja Isaki anasiliza kudalisa yakobo, na yakobo anachoka namata pamenso pa Isaki tate wake Esau mubale wake anabwela kuchokela mukugwila nyama. 31 Na eve anapanga chakudya chabwino nakuleta kuli batate bakee. Ana bauza batate bake, " Atate, ukani ndipo mudyeko nyama yamasanga ya mwana wanu,kuti mini dalise." 32 Isaki tate wake anakamba kuli eve, "ndiwe ndani?" anati, "Ndine mwana wanu mwamuna oyamba , Esau." 33 Isaki ananjenjema maningi nakukamba ati, "Nanga ni ndani wamene enze apaya nyama yamusanga nakuniletela? Ninali nadya yonse ukalibe kubwela, ndipo namudalisa uyo. Zo ona, uyu azankala odalisika." 34 Pamene Esau anamvela mau ya atate bake, analila maningi, mokalipa naku kamba kuti kuli batate bake, " Nidaliseni ine, naine batate banga." 35 Isaki anakamba, "Mubale wako enze abwela kuno monamiza, nakutenga madaliso yako." 36 Esau anakamba, "Uyu zoona zina yake si yakobo chifukwa aninama ine kabili anaipoka choyenela chaku badwa kwanga, ndipo, onani, manje atenga madaliso yanga. Ndipo anakamba, "Simunanisugileko daliso?" 37 Isaki anayaka naku kamba kuli Esau, "Ona, namupanga bwana wako, nakumupasa babale bake bonse monga ba nchito, ndipo na mupasa mbeu na vinyu ya sopano. Nanga nichani chamene ningakuchitila, mwana wanga mwamuna?" 38 Esau anakamba kuli batate bake, "Mulibe olo daliso imozi yanga, atate banga? Ni daliseni, naine, atate banga." Esau analila mo punda. 39 Isaki atate bake banayanka nakukamba kuli eve, "Ona, malo kwamene uzayenda kunkala yaza nkala ku tali na chuma cha ziko yapansi kutali na mame yakumwamba. 40 Kupitila mulupanga yako uzankala, naku sebenzela mubale wako. Koma ngati wamu ukila, uzachosa goli yake mu mukosi wako." 41 Esau anamuzonda yakobo chifukwa cha madaliso yamene bana mupasa batate bake. Esau anakamba mumutima wake, "Masiku yolila batate banga yali pafupi; yakapita nizamupaya mubale wanga Yakobo." 42 Mau ya Esu mwana mwamuna yana uziwa kuli Labeka. Ndipo anaitana Yakobo mwana wake mwamuna mungono naku kamba kuli eve, "Ona Esau azitontoza eka pali iwe pakuganiza ku kupaya iwe. 43 Manje, mwana wanga mwamuna, nimvelele ine nakutabila kuli Labani, mubale wanga, mu Halani, 44 Kankaleko na eve pangono, mpaka ukali wa mubale wako uchepeko, 45 mpaka ukali wamubale wako uchokeko kuli iwe, nakuibala vamene una chita kuli eve. Ndipo nizatuma nakuku bweza kuno. Nichifukwa cha chani niza kutayani bonse babili pa siku imozi? 46 Rabeka anakamba kuli Isaki, "Nalema nao umoyo chifukwa cha bana bakazi baku Heti ngati yakobo akwatila bana bakazi bena bana bakazi bakuno kumalo, umoyo wanga uzankala bwino bwnji?"