Mutu 28

1 Manje paku yenda kusila kwa Sabata, pamene kunayamba kucha siku yo yamba ya Sabata, Maria Madalena na uja Maria wina bana bwela kumanda. 2 Onani, kunali kungambika kwa ziko, chifukwa mungeli wa Mulungu anaseluka kuchokela kumwamba, nakubwela kuchosapo chimwala, naku nkalapo pachimwala. 3 Anali kuoneka monga kaleza, na vovala vake vinali votuba monga matalala. 4 Bolonda bana njenjema na manta naku nkala monga bantu bakufa. 5 Mungeli ana kamba nabo bazikazi naku bauza kuti, "Musayope, chifukwa ine niziba kuti musakila Yesu, wamene anapachikiwa. 6 Salipo pano, koma aukisiwa, monga mwamene anakambila. Bwelani muone pa malo pamene Ambuye banagona. 7 Endani mwa musanga muka bauze bopunzila bake kuti, 'Aukisiwa kubakufa. Onani, aenda akusogolelani kuyenda ku Galiyeya. Kwamene kuja muzamuona.' Onani, naku uzani." 8 Bakazi baja banachokako kumanda mwamusanga na manta mo kondwela kukulu, naku tamanga kuti bakauze bopunzila bake. 9 Onani, Yesu anaba kumana naku bauza kuti, "Moni!" Bazikazi banabwela, nakugwila mendo yake naku mupembeza. 10 Yesu anabauza kuti, "Musankale na manta. Endani mukabauze babale banga kuti bachokeko ku Galileya. Kwamene uja bazaniona." 11 Manje pamene bakazi banali kuyenda, onani, benangu pali bamalonda bana enda mumuzinda naku uza bakulu-bakulu bansembe vintu vonse vamene vinachitika. 12 Pamene ba nsembe banakumana na bakulu bakulu naku kambisana pali ichi chintu na beve, bana pasa ndalama zambili maning kuli ba silikali 13 naku bauza kuti, "Benangu mubauze kuti, 'Bopunzila ba Yesu benze bana bwela usiku ndishi ise tili gone nakuba tupi yake.' 14 Ngati iyi nkani yafika kuli ba kazembe, ise tizakamba nabo kuti imwe musa vutike mutima." 15 Mwa ichi baja basilikali bana tenga ndalama naku chita monga mwamene bana bauzila. Iyi nkani ina pelekewa maningi kuli ba Yuda bambili ndipo yapitiliza kufikila mpaka lelo. 16 Koma baja bopunzila banali kumi na umozi bana enda ku Galileya, ku pili yamene Yesu anabauza. 17 Pamene banamuona, banamupembeza, koma benangu banakaikila. 18 Yesu anabwela kuli beve naku bauza kuti, "Zonse mpavu zapasiwa kuli ine kumwamba na pansi. 19 Endani imwe muka pange bopunzila mu maiko yonse. Muba batize mu zina ya ba Tate, ya Mwana, na ya Muzimu Oyela. 20 Mubapunzise kuti bamvele vintu vonse vamene ine nina kuuzani. Onani, Ine nili naimwe ntawi yonse, mpaka kufikila kosilila ntawi."