MUTU 5

1 Alionse wamene akhulupilila kuti Yesu anabadwa kwa Mulungu, ndiponso wamene akonda tate ndiponso akonda mwana wamene anabadwa kwaiye. 2 chifukwa chaichi tiziba kuti tikonda bana bamulungu: ngati takonda ndi kuchita malamulo yamulungu. 3 ichi ndiye chikondi chamulungu: kuti tisunge malamulo yake. ndimalamulo yake siyolema. 4 Aliyense wamene anabadwa kwa Mulungu anagonjesa ZIKO.Ndiponso uku ndiye kupambana kuna gonjesa ziko: mwa chikulupililo chatu. 5 Ni ndani wamene angagonjese ziko? Iye wamene akulupilila kuti Yesu ni mwana wa Mulungu. 6 Uyu ndiye wamene ana choka ku manzi ndi ku mwazi: Yesu Kristhu.Sianabwele chabe na manzi, koma na manzi ndi mwazi. 7 koma kuli zitatu zamene zipeleka umboni: 8 Muzimu, manzi ndi mwazi. izi zitatu zimavomekezana. 9 Ngati talandila umboni kuchokela kubanthu, umboni wa mulungu ni wa ukulu. koma umboni wa Mulungu ndiye uyu ,kuti anapeleka umboni wa mwana wake. 10 Aliyense wamene akululupila mwana wa Mulungu alina umboni kwa iye eka.aliyense wamene siakululupila Mulungu azipanga eka kumkhala waboza, chifukwa sianakululupile umboni wamene mulungu unapasiwa kamba ka mwana wake. 11 Ndi umboni ni uyu: Mulungu anatipasa umoyo wamuyayaya, ndi uyu umoyo uli mu mwana wake. 12 wamene alina mwana wake alina umoyo.Iye wamene alibe mwana wa Mulungu alibe umoyo. 13 Nilembela izi zinthu kuti, kuti muzibe kuti mulina umoyo wamuyayaya__kuli imwe bamene bakulupilila mu zina la mwana wa Mulungu. 14 Ndiponso ichi ndiye chizindikilo chamene tili nacho mwa iye, kuti tikamufunsa chilichonse kulinganila na chifuniro chake, ama timvela. 15 Ndiponso, ngati amatimvela ise_ chilichonse chamene tizamufunsa_tiziba kuti tapasidwa chamene tamufunsa. 16 Ngati alionse aona mubale wake achita chimo yamene siipeleka kuimfa, afunika apempele, ndi Mulungu azamupasa umoyo. nikamba oaliaboabo bamene machimo yao siapeleka kuimfa. kuli chimo yamene isanduka ku imfa; sinikamba kuti anga pempele pali icho. 17 Zonse zamene siziliza ulungamo ni chimo, koma kuli chimo yamene siipelekaku imfa. 18 Tiziba kuti onse wamene anabadwa kwa Mulungu siamachimwa. koma uyo wamene anabadwa kuchokela kwa Mulungu amamusunga bwino kwaiyo eka, ndiponso uja woipa sianga muononge. 19 Tiziba kuti tichokela kwa Mulungu, ndiponso tiziba kuti ziko lonse zinkala muzoipa. 20 Koma tiziba kuti mwana wamulungu anabwela, ndiponso anatipasa kumvesesa uyo wamene ilina choonadi.koma, tilinaye wamene alina choonadi, mu mwana wake Yesu kristhu.Mulungu ndiye choonadi ndi moyo wamuyayaya. 21 Imwe bana, zichosenikoni kumafano.