Mutu 3

1 "Kwa mngelo wa ku Sardis lemba: Aya ni mau ya wamene asunga mizimu 7 ya Mulungu na nyenyezi 7." Niziba zamene mwachita. Muli na mbiri yakuti muli na moyo, koma ndinu bakufa. 2 Ukani na kulimbisa zamene zankhalako, koma zifuna kufa, chifukwa sininapezeko nchito iliyonse yabwino pamaso pa Mulungu wanga. 3 Kumbukirani, sopano, zamene munalandira na kumvera. Gonjerani, na kulapa. Koma ngati simuzauka, nizabwera monga kawalala, elo simuzaziba nthawi yamene nizabwelera kwa inu. 4 Koma pali maina yang'ono chabe ya banthu mu Sardis bamene sibanafipise vovala vao. Bazayenda naine, mu zobvala zoyera, chifukwa nioyenera. 5 Wamene apambana azapasiwa zobvala zoyera, elo sinizachosa dzina lake mu buku la moyo, ndipo nizakamba za dzina lake kwa atate, na angelo ao. 6 Lekani amene ali na matu amvere zamene mzimu akamba ku mipingo. 7 Kuli mungelo waku kachissi yaku Filadeofiya lemba: 'Mau ya uja wamene ni oyela nafuti wa zo-ona-wamene agwila mfungulo ya Davide, asegula ndipo kulibe wamene angakome, akoma ndipo kulibe wamene angasegule. 8 Niziba vamene munachita. Onani, Naika pameso pako chiseko choseguka ndipo kulibe wamene angachikome. Niziba kuti uli nato tumpavu tungóno, koma wakonka mau yanga suna kane zina yanga. 9 Onani! onse amene achokera ku mpingo wa satana, iwo amene akamba ati ni bayuda koma sibayuda; anama chabe boza. Nizabapanga kuti babwere bagwade pa mapazi yanu, ndipo bazaziba kuti nikukondani. 10 Chifukwa mwasunga malamulo anga mopilira, naine nizakusungani pa nthawi ya mayeso yamene ibwera padziko lapansi, kuyesa onse amene ankhala pa dziko. 11 Nibwera manje-manje. Sungani bwino zamene muli nazo kuti anthu asalande kolona yanu. 12 Nizapanga amene alimbikira kunkhala nsandamila ya mnyumba ya Mulungu, ndipo sazatulukamo. Nizalemba dzina la Mulungu pa iye, dzina la mzinda wa Mulungu wanga (Yerusalemu wasopano, wamene uchoka kumwamba kwa Mulungu wanga), na dzina langa lasopano. 13 Lekani wamene ali na matu amvere zamene mzimu ukamba ku mipingo. 14 Kwa mngelo wa mpingo wa ku Laodicea lemba: Aya ni mau ya ma Amen, mboni ya zoona na yodalilika, olamulira chilengedwe cha Mulung u. 15 Niziba zamene mwachita, kuti sindinu otentha kapena ozizira. Chinakankhala bwino kuti munali otentha kapena ozizira! Tsono, 16 chifukwa muli pakati-kati- simuli otentha kapena ozizira- nizakulabvulani mkamwa mwanga. 17 Mukamba kuti, ndinu olemera, nili na zinthu zambiri, ndipo sinifuna kalikonse. Koma simuziba kuti ndinu ochitisa chifundo maningi, osauka, osapenya ni osabvala. 18 Mvelani zamene nikamba: Gulani kwa ine golide oikidwa mu moto kuti munkhale olemera na zobvala zoyera zowala kuti mubvale musaonese manyazi ya umaliseche wanu, na mankhwala ya m'maso kuti uone bwino. 19 Nimazuzula aliyense wamene nikonda, ni kuwauza mwamene ayenera kunkhalira. Kotero, cita changu na kutembenuka. 20 Onani! naima pa khomo nigogoda. Ngati wina amvera mau anga na kusegulako, nizaloba mnyumba yake nakudya nayeve, yeve na ine. 21 Wamene apambana, nizamupasa mwai onkhala na ine pa mpando wa chimfumu, mwamene ine ninapambana na kunkhala na atate pa mpando wa chimfumu. 22 Lekani wamene ali na matu amvere zamene mzimu ukamba kwa mipingo.