MUTU 7

1 2 3 Kodi mwamuna samagwila nchito yokosa pa ziko yapansi? sikuti masiku aya ali monga masiku yamuntu wongenesewa nchito? monga wanchito mwamene amafunisisa vintuzi va usiku, monga muntu wanchito wamene amasakila malipilo yake- ndipo napangiwa kunkala mumasauso kwa myezi; Napasiwa usiku ozula mavwuto. 4 Nikagona pansi, nimakazikambisa neka, 'nizauka liti ndipo usiku uzayenda liti?' nazula ukoponyewa uku na uku kufikila pamene kuchela. 5 Nkanda yanga yavalikiwa navikusi na makuta ya fumbi; vilonda vili munkanda yanga vima yuma naku sungunuka nakuyamba futi. 6 Ma siku yanga yamatanga kuchila nsalu yoyenda; amapita kulibe nachiyembekezo. 7 Mulungu, kumbukila kuti umoyo wanga ni mpepo chabe; menso yanga siyazakaona chabwino nafuti. 8 Linso ya mulungu, wamene amaniona, sazakanionapo nafuti; menso ya mulungu yazankala pali ine, koma sinizankalako. 9 Monga kumbi mwamene idyeka nakusoba, ndiye kuti uyo wamene amayenda pansi ku shoeli siazabwela pamwamba futi. 10 Sazabwelela nafuti kunyumba yake; kapena malo yake kumuziba nafuti. 11 Mwaicho sinizalesa kamwa yanga; nizakamba mukubaba kwa muzimu wanga; nizadandaula mukubaba kwa moyo wanga. 12 Kodi ndine nyanja kapena chilombo chamunyanja kuti muikele wonilonda? 13 Nikakamba kuti, 'bedi yanga izanitontonza, na chipuna changa chiza chefya madandaulo yanga, 14 'mumaniyofya namaloto naku niyopesa mumasomphenya, 15 chakuti nisanke kukamiwa nakafa mumalo moteteza mafupa yanga. 16 Ninyanssidwa na umoyo wanga; siningafune kunkala wamoyo ntawi zonse; nisiyeni neka chifukwa masiku yanga yalibe nchito. 17 Muntu nichani kuti mumufakila nzelu, kuti muike maganizo yanu pali eve, 18 kuti muzimuyanganila kuseni kuli konse naku muyesa ntawi zonse? 19 Izankala ntawi itali bwanji mukalibe kuchosa menso pali ine, mukalibe kunisiya neka kwantawi itali chakuti nimele mate yanga? 20 Nangu nachimwa, Ivi vingakuchitileni chani, imwe bamene mumayanganila bantu? Nichani mwanipanga opingiliwa, chakuti ndine chilemeso chanu? 21 Nichani simumanikululukila volakwa vanga na kuchosa mpulupulu yanga? Pakuti manje nizagona pansi mu fumbi; muzani sakila mosamala, koma sinizankalapo,''