MUTU 6

1 Yobo anayanka nakukamba kuti, 2 ''Oho, ngati chabe masauko yanga yanali kupimiwa; ngait chabe masoka yanga yonse yayikiwa muchiyezo! 3 Pali manje chingankale cholema kuchila muchanga waku nyanja. Mwaicho mau yanga yanali yosasamaliwa. 4 Pakuti mivi ya wampavwu zonse ili muli ine; muzimu wanga umamwa poizoni; voyofya va mulungu vazikonzeka mu mzere kuimila ine. 5 Kodi bulu yamusanga imalila motaya mtima pamene ili na uzu? Kapena ng'ombe kunkala na njala pamene ili na chakudya? 6 kodi icho chosalawa chingadyewe kulibe muchere? kapena kuli kulawa kuli konse muli voyera vama dzira? 7 Nakana kuvigwila; vili monga vokudya vo nyansa kuli ine. 8 Oho, kuti ningankale na chofuna changa; oho, kuti mulungu anganipase chintu chamene nifunisisa: 9 kuti chinga kondwelese mulungu kuni shanyaula, kuti angalekele kwanja kwake nakunijuba kuchokela kuli umoyo wake! 10 Lekani ichi chinkalilile chitotonzo changa- nangu nimasangalala mukubaba kwamene sikumachepa: kuti sinakane mau yawoyera. 11 Kodi mpavwu zanga nichani, kuti niyese kuyenbekeza? Kodi nichani kusila kwanga, kuti ningatalimpise umoyo wanga? 12 Kodi mpavwu zanga ni mpavwu za myala? kapena nkanda yanda niyopangiwa na bulonzi? 13 kodi sivazoona kuti nilibe tandizo muli ine, ndipo kuti nzelu za chosewa muli ine? 14 Kuli muntu wamene alipafupi nakukomoka, ukulupililo ufunika kuoneka kuli banzake; nakuli wamene ataya manta ya wampavwu zonse. 15 Koma abale banga bankala bo kulupilika kuli ine monga musinje wachipululu, monga njila za manzi zamene zimapita pa chabe, 16 yamene yama fipisiwa chifukwa cha ayezi pamwamba pake, na chifukwa cha sinowo yamene imabisika mukati mwawo. 17 Yakasungunuka, yama soba; kukapya, yamasungunuka kochokela palo pake. 18 Ba paulendo bamene bamayenda munjila yao bama pita kukatunga manzi; bama yenda yenda mumalo yalibe kantu kali konse ndipo bama wonongeka. 19 Ba paulendobaku tema banayangana, pamene ma kampani ya Sheba yanankala nachiyembekezo muli beve. 20 Bana kumudwa chifukwa banali nachikulupililo chopeza manzi. Bana yenda, koma bana namiwa. 21 Pali manje imwe banzanga ndimwe bachabe kuli ine; mu ona kankalidwe koyofya kwanga nakuyopa. 22 Kodi ninamiuza kuti, 'munipase chintu' kapena, 'kunipasa mpaso kuchokela ku chuma chanu' 23 kapena, 'kunipulumusa kuchokela mumanja yabadani banga' kapena, 'kuniombola kuchokela mumanja yabonivutisa'? 24 Nipunziseni, ndipo nizagwila mutendere wanga; nitandizeni kuziba mwamene niluvyanya. 25 Mau yazoona yababa maningi bwanji! Koma kushusha kwanu, kunizuzula bwanji? 26 Kodi mufuna kuyalanyaza mau yanga, kuchitila mau ya muntu osimidwa monga mpepo? 27 Zoona, mumataya maelo yamwana alibe batate bake, ndipo mumasungila munzanu monga malonda. 28 Manje, mwaicho, napapata niyanganeni, chifukwa sininganame pamenso yanu. 29 Pepani, nekupempmani; pasankale chosalungama pali imwe; 30 Zoona, pepani, pakuti chifukwa changa nicholungama. Paliko voipa pa lulimi lwanga? pakamwa panga sipanga zindikile voipa