MUTU 28

1 Zoona kuli mugodi wa siliva, malo yamene bamapangila bwino golide. 2 Simbi amaitenga kuckela pansi; kopa aisungunula kucokela ku mwala. 3 Muntu amafaka cisilizilo kuli mudima na kusakila-sakila, mpaka ku malile ya kutali, myala ya mosazibika na mumudima ukulu. 4 Amasegula migodi kutali na kwamene bankala bantu, malo yamene yanaibaliwa na mendo ya aliyense. amapanyika kutali na bantu; nakupeluma kuja na kuno. 5 Monga kuli doti, kwamene kucokela buledi, imapilauliwa monga ni mulilo. 6 Myala yake ndiye malo kwamene safire imapezeka, na fumbi yake imanakala na golide. 7 Njila yamene iyi kuliba nyoni yamene iiziba, kapena nyoni yamene imafulumila maningi linso yake sinaionepo. 8 Nyama zozikweza inayendemo munjila monga iyo, kapena mkango woyofya kupitamo umo. 9 Muntu amafaka kwanja kwake pa mwala wombuwa; amapilaula malupili na mizhyu yake. 10 Amapanga njila pakati pa myala; menso yake yamaona ciliconse ca bwino maningi. 11 Amamanga misinje kuti manzi yaayende; camene cili cobisika kuja amacileta potuba. 12 Nzelu zingapezeke kuti? Nikuti kuli malo yakumvesesa? 13 Muntu saziba mtengo wake; kape kuti ipezek ku ziko ya ba moyo. 14 Pansi maningi pa manzi pansi pa ziko pakuti, 'sizili muli ine'; musinje ukuti, sizili na ine.' 15 Sizingaguliwe na golide; kapena kulemela kwa siliva kungankale mtengo wake. 16 Sizingalingane na mtengo na golide waku Ofiri, na oniki kapena safire. 17 Golide na kristo sizingalingane nazo; kapena kusintiwa na twamumukosi kapena kumanja twa goilide. 18 Kukamba zina ya korali kapena yaspa nikosayenela; zoona, mutengo wa nzelu niwopambana wa ndalama. 19 Topazi waku kusi sulingana nazo; kapena kulinganiza na golide wa bwino maningi. 20 Nikuti, manje, kucokela nelu? malo yomvesesa yali kuti? 21 Nzelu nizobisika mu menso ya camoyo ciliconse ndipo zimankala zobisika ku nyoni zakumwamba. 22 Cionongeko na imfa vikamba kuti, 'timamvela mbili cebe pali zeve na matu yatu.' 23 Mulungu amamvesesa njila za yeve; aziba malo yake. 24 Pakuti ayangana kosilizila kwake kwa ziko na kuona vonse vili pansi pa kumwamba. 25 Anapanga mpamvu ya mpepo na kuyesa manzi na muyeso wake. 26 Amalamulila mvula na kupanga njila ya kaleza. 27 Anaona nzelu nakuzilalikila; anazimapanga, zoona, nakuziyesa. 28 Kubantu anakamba kuti, 'yanganani, kuyopa kwa Ambuye-iyo ndiye nzelu; kucoka ku coipa ndiye kumvesesa."