Mutu 1

1 Yuda, kapolo ya Yesu Kristu, ndipo mubale wa Yakobo, kwa abo boitanidwa, ndi bokondedwa mwa Tate Mulungu wathu, ndi osungidwa mwa Yesu Kristu: 2 Ndipo chifundo, mutendere ndi chikondi viyonjezelwepo pa inu. 3 Bokondedwa, pamene nenze kuyeselela na mphavu zanga zonse kuti ndilembe kwa imwe pankaani ya chipulumuso chathu tonse, chenzo ufunika kuti nikulimbikiseni kuti muvutikile chi khulupiliro chamene chinapasidwa kwaise pa thawi imozi na mitima zanu zonse. 4 Chifukwa bantu bena babwela kwainu mwakabisila. Aba bantu banakonzekedwa ku kulangiwa. Ndipo nibantu bochimwa bamene beendeka chisomo cha Mulungu watu nochipeleka muuchisilu, ndipo bakana Ambuye Mfumu yatu, Yesu Kristu. 5 Apa nifuna kukukumbusani - olo kwenze ntawi ina mwenze bochiziba chonse - kuti Ambuye anapulumusa bantu ba ku Egipito, koma kuchoka paja anabaononga baja bamene sibanakhulupilire. 6 Ndipo bangelo bamene sibanasunge mushe udindo wao wa ulamulilo, koma banasiya mhalo yamene benzofunika kunkhalapo - Mulungu anabamanga mumupata wa muyayaya, muminyololo mo fipa, abasungila siku ija ikulu yoweruuza. 7 Monga Sodoma na Gommora ndi mizinda nzezo bazunguluka, zinachita vigololo ndiponso zichita zina zosayenera kuchitiwa ndi antu. Banabaika chisanzo cha baja bamene banasunzika kuvutika mu moto wosata. 8 Manje munjila imozi na imozi aba ba maloto baononga ma tupi yabo. Bamakana ulamulilo, ndipo bamakamba zoipa pali abo ba ulemerelo. 9 Koma na Mikayeli mukulu wa angelo, pamene enze kusushanya na Satana pa tupi ya Mose sana yese kumuuza choyipa yayi. Koma anamuuza kuti, "Ambuye akuzuzule!" 10 Koma aba bantu ba makamba vo kambakamba pa zitu zilizonse zamene sibaziba mushe. Ndipo baziba chabe - monga vinyama vosaganiza viziba muchizibiso - ivi ndiye vinabaononga. 11 Soka kwa eve! Chifukwa banayenda njila ya Kaini, ndipo banizingenesa muku lakwa kwa Balaamu kofuna kudyelamo. Banaonongekela mu kupanduka kwa Korah. 12 Aba ndiye bamene bazibisa mumagulu ya ma pwando yachikunja. Ba ma kondyelela kopanda nsoni, bangozidwesa bene beka. Nimakumbi yalimbe manzi, otengewa chabe na mpepo. Ni mitengo zamu ntawi yo panda mvula zilibe vipaso - bokufa kabili, bong'ámbika na mizu. 13 Ndi mafuunde oyipa pa chimana, bopanga manyazi yabo. Ni nyenyezi zosokera, zimene mudima wakuda unusungiwa masiku osasila. 14 Enocki, wa nambala seveni kuchoka pa Adam, anapa uneneri pali beve ati, "Onani! Ambuye abwera ndi banthu bambiri makaana na makaana nabo yela bake. 15 Abwera kupasa chiwerudzo pamunthu onse. Abwera kugojensa bonse bamene bachita nchito zoyipa zamene bachitila mukuyipa kwao, ndipo na mau onse ya ntota yamene aba ba machimo banakamba kwa iye. 16 Aba bang'ung'uza, ba madandaulo, bamene bakonka zifunilo zao za uchimo. Ndipo ni bozinvela, bamene pakuti vintu vibayendele mushe bekabeka, bama tilimula ba nzao. 17 Koma, inu bokondedwa, kumbukani mau yamene Ambuye Yesu Kristu anakamba ku mbuyo uku kupitila mu atumwi. 18 Banakamba kwainu ati, "Mu ntawi yo tera kuzankala banthu boseka chikulupiliro bamene bazakonka zifunilo zawo za uchimo." 19 Aba banthu nibopatukisa. Bakonda za muziko, ndipo balibe Muzimu. 20 Koma inu bokondedwa, zimangeni nhoka muchi khulupirilo chanu cho yela ngako, ndipo mupempele mu Muzimu Oyela. 21 Zisungeni mweka mu chikondi cha Mulungu, ndipo yembekezelani chifundo cha Ambuye watu Yesu Kristu chamene chileta umoyo osasila. 22 Nkalani na chifundo kwaibo bamene sibanakhulupirile. Pulumusani bena ndikubachosa mumulilo. 23 Kuli bena munkhale ba chifundo ndi kuyopa. Muzondenso na zovala zotimbiridwa za tupi. 24 Manje kuli iye akwanisa ku khusungungani kuti musazibuntule, ndipo ku pangani kuti muyimilile mu mhalo yake ya ulemerero wake, kulibe kusekewa ndipo nakunkala na chimwemwe chapitilila, 25 kuli Mulungu umozi eka Mupulumusi watu kapitila mwa Yesu Kristu, Mfumu yatu, kunkhale ulemerero, ndi ulamurilo, ndi mphavu, nthawi ikalibo yamba, ndi manje, ndi ntawi zonse. Ameni.