Mutu wachitatu

1 Mwaichi' imwe okwatiwa nvelelani ba muna banu. Chitani ichi nangukuti amuna banu samvelela mau, an'nga tembenuke nangu kulibe mau, mukupitila muzochita za bakazi bao. 2 Baza ona zochita zao zabwino za ulemu. 3 Asachite nazo onekela kunja: nazibango zovala kumanja za golide na zovala. 4 Mumalo mwake lekani zichitike na mtima wonse, naku kongola kwa bwino kwa mu mzimu, yo kongola kwa Mulungu. 5 Pakuti azimai oyela anamu lemekeza munjila iyi. Bana limbikila mwa Mulungu kunvelela amuna bao. 6 Munjila iyi Sala ananvelela mwamuna wake Aburam naku muitana ambuye, ndimwe bana bake pamene munvelela cha bwino, napa mene simuyopa mavuto. 7 Munjila imozi mozi naimwe ba muna mu nkhale nabagazi banu muku nvelana, monga mukazi niofoka. Mukaziba pasa ulemu monga nibamozi ba nchito na mpaso mu umoyo.Chitani ichi kuti ma pempelo yanu ya yankhiwe yasa chingiliziwe. 8 Naposiliza, imwe monse,nkalani ba maganizo yamozi, ba chifundo bokondana, ba mitima yabwino. 9 Osabwezela choipa pa choipa naku tukwana paku tukwana, osa chita izo pitilizani ku dalisa chifukwa chaichi muna itanidwa, kuti mutenge daliso. 10 Amene akonda umoyo wabwino nakufuna kuona zabwino asiye kunena nalilime zoipa zama boza. 11 Achoke ku choipa achite chabwino, afunne mtendele aupilikise. 12 Menso ya Mulungu yaona oyela, namatu yake yanvela zopempa zao. Koma chinso cha Mulungu chimaukila ochita zoipa.'' 13 Ni ndani azakuchitani choipa ngati mukonda zabwino? 14 Koma ngati muvutika chifukwa chakuyela, ndimwe odalisika. Osayopa zamene ba yopa, osa vutisika. 15 mumalo mwake, ikani Yesu pakati mu mutima mwanu mo yeleseka. Nkalani oko nzenka ntawi zonse pamene mufunsiwa chifukwa nchani mulimbikila mwa Mulungu. Chitani izi mozichepesa na mwaulemu. 16 Nkhalani namaganizo yabwino kuti bantu okunenani pa umoyo wanu wabwino ba nvele nsoni pazamene muchita zabwino. 17 Nicha bwino ngati Mulungu afuna, mu vutike pakuchita chabwino osati choipa. 18 Klistu naye ana vutika chifukwa chama chimo yatu. Eve oyela anatifela, enze oyela, kuti ati bwelese kwa Mulungu. Ana paiwa kumubili koma anauka kumuzimu. 19 Mwa muzimu, anapita kulalikila kuba mu ndende. 20 Sibana nvelele pamene Mulungu anaba yembekezela mumasiku yanowa. Mumasiku yopanga chi boti na Mulungu ana pulumusa bantu ban'gono-moyo zili chabe 8. kupita mu manzi. 21 Ichi ndiye cho oneselako kubatizika kwanu kwa manzi, kubatiza koku pulumusani manje -siku suka monga kwa doti mumubili, koma cho onesela ganizo yabwino ya Mulungu, kupitila muku ukisidwa kwa mwana wake Yesu Klistu. 22 Yesu ali ku kwanja ya Manja ya Mulungu. Ana yenda ku mwamba. Ba ngelo, bolamulila, nampanvu zikazimuvelela.