Mutu 7

1 Mendo yako ya oneka yokongola bwanji mu nsapato zako, mwana wa mukazi wa fumu! Kubenda kwa vibelo vako vioneka bwino, yokongola monga myala yo kongola, nchito ya manja ya kaswili wavo panga panga. 2 Muhombo wako uli kwati mubale mozunguka; lekani isakasobe vinyu vosankaniza. Mimba yako ili kwati cho umba cha tiligu chozunguluka na maluba. 3 Mabele yako yabili yali monga bana ba bili ba insha. 4 Mukosi yako uli kwati nsanja nyanga ya njovu; menso yako ya nyezimila manzi yaku Hesiboni , pafupi na chipata cha Bath Rabbim. Mpuno yako ili kwati nsanja ya ku Lebanoni yamene iyangana ku Damasika. 5 Mutu wako uli pa iwe kwati Karimeli; sisi yaku mutu kwako ni lofiilila. Mfumuyo imagwidwa ukapolo ni zikakamizo zake. 6 Okongola, ndiwe okongola bwanji, okondewa wanga! 7 Kutalimpa kwako kuli kwati mutengo wa kanjeza, ndipo mabele yako yali kwati gulu ya ba paso. 8 Nina kamba kuti, "Nifuna kukwela mutengo wa kanjeza; nizagwila misabo zake." Mabele yako ya nkale kwati zipatso za mphesa, Ndipo fungoyla mpuno yako inkale kwati apulikoti. 9 Pakamwa pako pakale kwati vinyu yabwino, Yo konkoloika bwino okondewa wanga, oyenda pa milomo ya bali gone. 10 ndine wa okondewa wanga, ndipo amani lakalaka. 11 Bwela, okondewa wanga, tiye tichoke muziko; tiye tika gone mu munzi. 12 Tiye tiuke kuseniseni tiyende ku minda ya mphesa; tiye tikaone ngati mipesa yaphuka, kaya maluba yake yaseguka, kapena ngati makangaza yali na maluba. Kwamenekuja niza kupasa chikondi changa. 13 Zipaso za makwala za chikondi zipeleka kununkila kwake; pogenela pamene tinkala pathu pali zipaso zamitundu mitundu zabwino,za manje na za kudala, zamene nakusungila iwe, okondewa wanga.