Mutu 21

1 elo ninaona kumwamba kwasopano na ziko lapansi lasopano, cifukwa kumwamba na ziko ya kudala vinapita, na nyanja sizinaliko. 2 ninaona muzinda oyera, yerusalemu wa sopano, zamene zinachoka kumwamba kwa mulungu, kukonzewa monga mkazi wamene akumana na mwamuna wake. 3 ninamvera mau yochokera ku mpando kukamba kuti, "onani! malo yamene mulungu ankhalako yali na banthu, elo azankhala nabeve. bazankhala banthu bake, elo mulungu mwini wake azankhala nabeve elo azankhala mulungu wao. 4 azapukuta misozi yawo yonse mumenso mwawo, elo sikuzankhala kufa, kulira, kapena kudandaula, kapena kuwawa. zinthu zakudala zapita. 5 wamene anankhala pa mpando anakamba ati, "ona! nipanga zinthu zonse zasopano." anati, "lemba izi pansi chifukwa mau aya ni ya zoona." 6 anakamba naine ati, "izi zinthu zasila! ndine alefa na omega, oyamba na osiliza. kwa wamene amvera njota nizamupasa manzi yosagula kuchoka ku musinje wa manzi ya moyo. 7 wamene apambana azatenga zinthu zimenezi, elo ine nizankhala mulungu wake, yeve azankhala mwana wanga. 8 koma bamene bachita mantha, opanda chikulupiliro, na okanika, wopaya anzao, bachigololo, ba boza, opembeza mafano malo yawo ni ku nyanja ya muliro wa sufule. iyi ni imfa ya chiwiri." 9 m'mozi wa angelo bali 7 anabwera kwa ine, wamene anali na mbale 7 zozula na zilango zosiliza, anakamba kwa ine, "bwera kuno. nizakulangiza mkazi, mkazi wa mwana wa nkhosa." 10 ananitenga mu mzimu kuyenda ku lupili itali nakunilangiza muzinda oyera yerusalemu kuseluka kuchoka ku mwamba kwa mulungu. 11 yerusalemu anali na ulemelero wa mulungu, na kuwala kwake kunali monga mphete, monga mwala wa bafuta wa jesipa. 12 unali na mpanda waukulu, na polowera 12, na angelo pa khomo. pa makomo onse panalembewa maina ya mitundu 12 ya ana a israele. 13 ku m'mawa kunali makomo atatu, kumpoto kunali makomo atatu, ku m'mwera kunali makomo atatu komanspo kumazulo kunali makomo atatu. 14 mpanda wa mzinda unali ni maziko 12, pa izo panali maina 12 ya apositoli a mwana wa nkhosa. 15 wamene anakamba na ine anali na kopimila kopangiwa na golide kamene anapimila mzinda, makomo na mpanda wake. 16 mzinda unali olingana mbali zonse; utali wake unali olingana na ukula kwake. anapima mzinda na kopimila, 12000 kutalika kwake (kutalika, m'mimba ni kukula kwake kunali chimozi-mozi). 17 anapimaso mpanda wake 144 cubits unenepa kwake kulingana na kupima kwa munthu (komwe ni kupimanso kwa mngelo). 18 chipupa chinamangiwa ni jesipa na mzinda wa golide, monga galasi yowala. 19 maziko ya chipupa yanali yomangiwa na minyala ya mtengo odula. 20 oyamba unali jesipa, waciwiri safire, wacitatu agate, wacinai emalodi, wacisanu onyx, wa 6 carnelian, wa 7 chrysolite, wa 8 ni beryl, wa 9 unali topaz, wa 10 chrysoprase, wa 11 unali jacinth ndipo wa 12 ni amethyst. 21 makomo 12 yanali ya pearls; khomo ilkiyonse inali yopangiwa na pearl imozi. miseu ya mu mzinda yanali yopangiwa na golide, monga galasi. 22 sininaone tempile mu mzinda, chifukwa mulungu na mwana wa nkhosa ndiye tempile yawo. 23 mzinda sumafunika zuba kapena mwezi kuti uwunike cifukwa ulemelero wa mulungu unaunika, ndipo nyale yawo ni mwana wa nkhosa. 24 maiko yazayenda kulingana na nyale ya mzinda. mamfumu ya pa ziko yazabweresa kuwala pa iyo. 25 makomo yake siyazavaliwa muzuba ndipo sikuzankhala usiku. 26 yazabweresa kuwala na ulemu ku maiko ya mkati, 27 ndipo kulibe chodesewa chamene chizangenamo. kapena aliyense wamene achita zinthu zocitisa manyazi kapena za chinyengo sazalowa, koma bamene maina yawo yanalembewa mu buku ya mwana wa nkhosa.