Mutu 18

1 izi zitasila ninaona futi mungelo winangu aseluka kuchoka ku mwamba. anali na mpamvu zambiri, elo ziko inawala kamba ka ulemelero wake. 2 anapunda na mau yakulu, kukamba ati, ̈̈agwa, agwa babylon wa mpamvu! wankhala malo yonkhalako ziwanda, konkhala mizimu yoipa na kobisala mizimu yonyansana nyoni zosaloledwa. 3 kabili maiko yonse yamwa vinyo wa chigololo. mamfumu ya muziko yacita chigololo nayeve. bantu ba paziko balemela na mpamvu za nkhalidwe yake yoipa." 4 ninamvera futi mau yenango kuchokera ku mwamba kukamba ati, ̈ chokako kuli eve, bantu banga, kuti musatengeko mbali mu machimo yake, kuti musabvutisiwe na manzunzo yake. 5 machimo yake yapaka kufika ku mwamba, elo mulungu akumbukira zocita zake zoipa. 6 bazamupasa mwamene eve anapasila benango, na kumupasa vambiri pa vamene anacita; mu kapu yamene anasakaniza, sakanizani kawiri za yeve. 7 pamene anazikweza yekha na kunkhala pa mushe, musauseni maningi kuti ankhale odandaula. chifukwa amakamba mu mtima mwake ati, 'nankhala kwati ndine mfumukazi; sindine ofedwa elo sinizakalilapo.' 8 Manje siku izabwera yamene mabvuto yake yazabwera: imfa, kulira na njala. asafa na mulilo, chifukwa mulungu ni wa mphamvu, elo ndiye wamene azamuweruza.̈ 9 mamfumu ya pa ziko yamene yanacita chigololo nokangiwa kuzilesa bazamulira elo bazaona chusi cha kupya kwakw. 10 bazaimilira patali, kuyopa kuonongeka kwake, bazakamba ati, ̈ tsoka, tsoka kwa muzinda waukulu, babylon, muzinda wa mpamvu! pakuti pa ola limozi chabe chilango chafika.̈ 11 anthu ba paziko balilira yeve chifukwa kulibe wamene agula zinthu zao- 12 zitu za golide, siliva, minyala yodula, nsalu, mitengo yonunkila mbiya za minyanga na zinangu zopangidwa na zinthu za mtengo wa patali, 13 cinamon, zonunkhirisa, mafuta, fulawo, tirigu, ng'ombe na nkhosa, mahosi na akavalo na akapolo elo na mizimu ya banthu. 14 zipaso zamene mwenze kufuna na mpamvu zanu zonse zakusiyani. zonse zabwino zayenda ndipo sizizapezeka nafuti 15 katundu wa aba bamene banalemela kamba ka uyu uzaimilira kutali kamba ka mantha ya kuvutisiwa, kulira mokuwa. 16 bazakamba, ̈ tsoka, tsoka ku mzinda wampamvu wamene wenze unavalikiwa zovala zabwino, zabafuta komanso za golide, mphete zabwino! 17 pa ola imozi chabe katundu onse waonongeka.̈ osogolera aliyense wa bwato, aliyense oyendesa bwato na aliyense amene ankhalira zinthu zamene zinkhala pa manzi, zinaimilira patali. 18 banalira pamene banaona chusi cha kupya kwake. banakamba ati, ̈ ni muzinda wabwanji wamene uli ngati muzinda wampamvu?̈ 19 bataya dothi pa mitu zao, na kulira mwampamvu, ̈ tsoka, tsoka ku muzinda wa mphamvu wamene bonse benzeli na bwato banalemela na chuma chake. pakuti pa ola imozi chabe aonongeka.̈ 20 kondwerani na yeve, kumwamba, inu okulupilira, atumwi na apolofeti, pakuti mulungu abweresa chiweruzo pa yeve!̈ 21 mungelo wamphamvu anatenga mwala owoneka kwati ni chogailapo na kuuponya mu manzi, kukamba ati, ̈ pa sochabe, babylon, muzinda wa mpamvu uzaponyedwa na ndewo zake ndipo suzaonekanso. 22 Zoimba zopangidwa ndi oliza mitolilo, oimba nyimbo ndi malipenga sazamvekaso pa inu. palibe munthu aliyense wa maluso sazapezeka pakati panu. palibe chigayo chamene chizamveka pakati panu. 23 nyale sizawalanso pakati panu. mau ya mkwati ndi mkwatibwi siyazamvekanso pa inu, pakuti banthu banu banali mamfumu pa ziko lapansi, elo maiko yananamiziwa na ung'anga wanu. 24 muli yeve magazi ya aneneri na okulupilira yanapezeka, na magazi ya onse bamene banapaiwa pa ziko.̈