Chapita 22

1 Panthawi inja, Yoswa anaitana Arubeni, A Gadites, na mutundu bogabika pakati wa manase. 2 Ananakamaba kuli beve,'' mwacita vonse vamene Mose mutumiki wa Yeehova anakulamulila iwe, wamvelela mau yanga mu vonse nina kulamulila. 3 Sunasiye abale ako masiku aya, paka kufika nalelo, na kukwanilisa nchito zofunika mwa malamulo ya Yehova mulungu wanu. 4 Manje Yehova mulungu wako apasa kupumula kuli abale bako, monga mwamene anabalonjezela. cifukwa chake bwelelani nakuyenda kumahema yanu mu malo yanu, yamene Mose mutumiki wa Yehova anakupasani kumbali ina ya Yolodani. 5 Khalani bo bonesesa kukonkha malangizo na namalamulo yamene Mose mutumiki wa Yehova anakulamulila iwe, kukonda Yehova mulungu wako, kuyenda munjila zake zonse, kusunga malamulo yake yake, nakulamatila kuli yeve na kumulambila namitima wako bonse na moyo wako bonse.'' 6 Pomwepo Yoswa anabadalisa na kubatuma, ndipo banabwelela ku mahema yabo. 7 Manje kuli imozi ya mutundu bogabika pakati wa manase Mose anapasa coloba mu Bashani, koma kumbali ina Yoswa anapasa coloba pambali namubale wabo mumalo yakumazulo kwa Yolodani. Yoswa anababuza kuti bayende kumahema yabo; anabadalisa 8 nakukamba nabeve,'' bwelelani kumahema yanu na ndala zambili, na vobeta vambili, na siliva na Golide, na Bronzi na nsimbi, na vovala vambili. Gabana votenga kuli badani banu na ba bale banu. 9 Ndipo bana ba Rubeni, bana ba Gadi, na mutundu bogabika pakati wa manase unabwelela kunyumba, kusiya banthu ba Israyeli pa shiloh, yamene ili muziko ya kanani. Banacoka kuyenda kucigabo ca Gileadi, kumalo yabo, yamene beve banatenga, mukumcelela kulamulo ya Yehova, mwa kwanja kwa Mose. 10 Pamene banabwela ku Yolodani yamene ili muziko ya kanani, A Rubeni na ba Gadites na mutundu bogabika pakati wa manase unamanga guwa pambali ya Yolodani, guwa yaikulu yamaonekedwe yabwino. 11 Bana ba Israyeli banamvela pali ivi nakukamba kuti,'' ona! banthu ba Rubeni, Gadi, na mutundu bogabika pakati wamanase bamanga gua kusogolo kwaziko yakanani, pa Geliloth, mucigabo pafupi na Yolodani, kumbali ya bana ba Israyeli.'' 12 Pamene bana ba Israyeli bana mvela pali ici, musonkhano bonse bwa banthu ba Israyeli unakumana pamozi pa shiloh kuyenda kuwamba kukamenya nkhondo nabeve. 13 Ndipo bana ba Israyeli banatuma amithenga kuli A Rubeni, A Gadites, na mutundu bogabika pakati wa Manase, mumalo ya Gileadi. Banatumanso phlnehasi mwana wa Eliyaza, wa nsembe, 14 Pamozi nabosogoleli bali teni (10) umozi kucokela kumutundu wa mabanja ya Israyeli, na alibonse wa beve anali musogoleli wabanja pakati ka mabanja ya Israyeli. 15 Banabwela kuli bana ba Rubeni, Gadi, na mutundu bogabika pakati wa manase, muziko ya Gileadi, ndipo anakamba nabeve: 16 Musonkhano bonse wa Yehova ukamba izi,' nicani ici cosa khulupililika camene wacitila mulungu wa Israyeli, pakucinja munjila iyi siku yalelo kuleka kukonka Yehova na kuzimangila imwe mweka guwa lelo yo bukila mulungu? 17 Kodi cima yathu pa peor sinali yakwanila kwa ife? Koma sitinaziyeleta kucima, Popeza pacimo ija panabwela mulili pa msonkhana wa Yehova. 18 Naiwenso ufuna kuleka kukonka mulungu pasiku yalelo? Ngati uzaukila nso mungu naiwe lelo, mailo azakalipa na musonkhano bonse wa Israyeli. 19 Ngati malo yamene ulinayo yabonongeka, mufunika kupitila muziko mwamene cihema ca Yehova cikhala na kuzitengela vinthu pakati kathu. Imwe osabukila mulunngu, kapene ife pakumanga guwa yanu malo momanga ya Yehova mulungu. 20 Kodi Akani mwana wa Zera sana phanye cikhulupililo muvinthu viji vinasunguwila mulungu? mukwiyo sunagwele bana ba Israyeli? Uja munthu sanabongeke yekha pa zolakwa zare. 21 Pamene mitundu ya A Rubeni, Gadi, na mtundu bogabika pakati wa manase unayankha kuli asogoleli ba mabanja ya Israyeli: 22 Waphamvu, mulungu, Yehova! Wamphamvu mulungu, Yehova! - Aziba, lekeni Israyeli azibe! ngati zinali mukuukila kapene mukuphwanya cikhulupililo ca Yehova, Osatisiyako siku iyi. 23 Pamanga guwa kuzicosa ise teka kukonka imwe Yehova. Ngati timanga guwa cifukwa copeleka nsembe zopseleza, nsembe za ufa, kapene nsembe zamtendele, pamenepo lekan Yehova atilipise. 24 Kapena! tinacita ici kuyopa kuti mu nthawi yobwela ba banu bangakambe kuli bana banthu,' muli cini imwe kuli Yehova, mulungu wa Israyeli? 25 Popeza Yehova apanga Yolodani malile pakati pathu na imwe. Imwe banthu ba Rubeni na bathu ba Gadi, mulibe vocita na Yehova.' cifukwa cake bana banu angale ngese bana bathu kuleka kulambila Yehova. 26 Cifukwa cake tinakamba, tiyeni manje timange guwa, osati ya nsembe zopseleza kapene ya nsembe zili yonse. 27 Koma kukhala mboni pakati pa ise naiwe, na pakati mibadwa yakusogolo kwathu, kuli tizacita nchitoya Yehova pamenso pake, na nembe zathu zopsele na nsembe zathu na nsembe zathu zamtendele, kuti bana bako sazakamba kuli bana bathu munthawi yobwela,'' mulibeve mbali mu Yehova.''' 28 Ndipo tinakamba kuti, ngati izi zifunika kukambiwa kuli ise kapena kuli bana bathu munthawi yobwela, tingakambe kuti,''' onani! Ici cisanzo caguwa ya Yehova, yamene makolo bathu banapanga, osati ya nsembe zopseleza, kapene nsembe, koma monga mboni pakati kathu naimwe.'' 29 Zikhale patali naise kuti tiukile Yehova, nalelo kuleka kumukonka iye pakumanga guwa ya nsembe zopseleza na nsembe zaunga, kapenazansembe, mumalo ya guwa ya Yehova mulungu yamene ili pasogolo ya cihema. 30 Pamene phinehasi wansembe na basogoleli ba banthu, bamene, basogoleli ba mabanja ya Israyeli bamene banali naine, banamva mau yamene banthu ba Rubeni, Gadi na manase banakamba, kuti yanali bwino mumenso. 31 Phinehasi mwana wa Eliyaza wansembe anakamba kubanthu ba Rubeni, Gadi, manase,'' Lelo tiziba kuti Yehova ali pakati pathu, cifukwa simuna phwange cikhulupililo ca Yehova. Manje mwa pulumusa bana ba Israyeli kucoka mumanja ya Yehova. 32 Pamenepo phinehasi mwana wa Eliyaza wansembe nabasogoleli banabwelela kucoka ku A Rubeni na A Gadites, kucoka muziko ya Gileadi, kubwelela muziko ya kenani, kuli bana ba Israyeli, naku bwelesa mau kuli beve. 33 Mayo yabo yanali ya bwino mumenso ya bana ba Israyeli, Bana ba Israyeli banadaalisa mulungu nakusa kamba ponso zomenya nkhondo naba Rubeni na ba Gadites, kuti babonge malo mwamene bana nkhala. 34 A Rubeni naba Gadites anapasa zina guwa kuti.'' Mboni popeza banakamba,'' ni umboni pakati kathu kuti Yehova ni mulungu.