MUTU 2

1 Mwaicho inali siku yamene bana bamulungu bana bwela kuziwonesa pa menso ya Yehova. Satana nayeve anabwela nabeve kuziwonesa kuli Yehova. 2 Yehova anakamba kuli satana,'' Nikuti kwamene wachokela?'' ndipo satana anayanka Yehova nakukamba kuti, '' Nachokela muyendayenda paziko ya pansi, kuchokela pambuyo na pasogolo.'' 3 Yehova anakamba kuli satana kuti, '' wamuganizila wanchito wanga Yobo? pakuti kulibe muntu wamene ali monga eve paziko ya pansi, mwamuna wamene alibe mulandu ndipo owongoka, wamene ayopa mulungu nakutaba voipa. Akali kugwilila umpup wake , ngakale unani sochelesa kumuononga palibe nachifukwa.'' 4 Satana anayanka Yehova ndipo anakamba kuti, '' Nkanda pa nkanda, nditu; mwamuna angapasa vonse vamene alinavo pali umoyo wake. 5 Koma tambusula kwanja yako manje na kugwila mabonzo yake na tupi yake, na kuona ngati eve sazakutembelela pa menso yako.'' 6 Yehova anakamba kuli satana kuti,'' Ona, alimunja yako; niumoyo wake chabe wamene ufunika kusiya.'' 7 Ndipo satana anayenda nakuchoka pamenso ya Yehova. Anakanda Yobo na vituzi vobaba maningi kuchokela kunsi kwamendo yake kufikila kumutu wake. 8 Yobo anatenga chidunswa cha chobumba kuti azikolole, ndipo anankala pakati pa milota. 9 Mukazi wake anakamba kuti kuli eve,'' kodi ukali kufuna kugwilila kuli umuntu wako? Tembelela mulungu nakufa.'' 10 Koma anakamba kuti kuli eve, '' Ukamba monga mukazi opusa mwamene amakambila. Tilandile vabwino kuchokela kuli Yehova ndipo osati voipa? munkani iyi yonse, Yobo sanachimwe na milomo yake. 11 Manje pamene banzake ba Yobo batatu bananvela pali vonse voipa vinabwela pali eve, aliyense anabwela kuchokela kumalo yake: Elifazi waku temaniti, Bilihadi waku shuhiti, na Zofa waku Naamatite. Banakonza ntawi kabwela kulila naeve kumulimbisa mutima. 12 13 Pamene bana nyamula menso yao chapali, sibanamuzibe. Bananyamula mau yao nakulila; aliyense anang'amba mukanjo wake nakuponya fumbi mumnpepo napa mutu pake.Banankala nayeve pansi kwamasiku yali 7 na usiku 7. Kulibe anakamba mau kuli eve, chifukwa banaona kuti anali muchisoni chikulu maningi.