MUTU 10

1 Ndine ozuzika na umoyo wanga; nizapasa dandaulo yanga momasukila; Nizakamba mu kubaba kwa umoyo wanga. 2 Nizakamba kuli mulungu, 'usani nyoze chabe; nilangiseni chifukwa chamene muninamizila. 3 Nichabwino kuli imwe kuti muzinikakamiza, kunyoza nchito ya manja yanu pamene musekelela pali ma mapulani ya boipa? 4 Kodi uli na menso ya tupi? Kodi umaona monga muntu mwamene amaonela? 5 Kodi masiku yako yali monga masiku ya bantu kapena zaka zanu monga zaka za bantu, 6 kuti mufunikiza pali vakulakwa kwanga na kusakila chimo yanga, 7 ngakale muziba kuti sindine olakwa ndipo kulibe aliyense wamene anganipulumuse kuchokela mumanja yanu? 8 Manja yako yanipanga nakunipyata pamozi kunizangulukila, koma muniononga. 9 Kumbukilani, nakupapatani, kuti mununanipanga monga doti; muzani bweza muli fimbi nafuti? 10 Kodi simuna tile monga mukaka nakuni ni juba monga chizi? 11 Wanivalika na nkanda na mnofu na kuintunga pamozi na mabonzo na miyewa. 12 Wanipasa umoyo na chipangano chokulupilika; tandizo yanu ya teteza muzimu wanga. 13 Koma ivi vintu una bisa mumutima wako- niziba kuti ivi nivamene wenze kuganiza: 14 kuti ngati nachimwa, mungazibe; simungani kululukile pali volakwa vanga. 15 Ngati nachita voipa , soka kuli ine; ndipo olo ngati ninachita mwachilungamo, sinina nyamule mutu wanga, popeza nazuzidwa na manyazi- onani mazunzo anga! 16 Ngati mutu wanga wanyamuliwa pamwamba, mungazini langana monga mkango; ndipo nafuti mungazini onesa na machitidwe ya mushe ya mpavwu pali ine. 17 Muma leta mboni za sopano kushushana naine na kukwezeka ukali wanu naine; mumani menya na magulu ya nkondo ya sopano. 18 Nichani, ndipo, mwanichosa mumala? nilikulakalaka ninasiya muzimu wanga ndipo kuti kulibe linso iliyense yamene inaniwonapo. 19 Ningankale ngati sinina onekepo; ndikananyamulidwa kuchokela mumimba kupita kumanda. 20 Kodi masiku yanga siyali chabe yang'ono? lekani pamene apo, nisiyeni neka, chakuti nipumuleko pang'ono 21 nikalibe kuyenda kwamene sinizabwelela, ku malo ya mudima na chintuzi cha infa, 22 malo yamene yofipa monga pakati pa usiku, malo ya chintuzi cha infa, kulibe kulongosoka, kwamene nyali ili monga pakati pa usiku.'''