Mutu 18

1 Davide anabapenda basilikali bamene banali nabo naku basanka bazisogoleli bali sauzande naba sogoleli bali handred pali benve. 2 Chokonkapo Davide anatuma ba nkondo, anaba gaba muma gulu yatatu pali olamuliliwa kuli Yowabu, nama gulu yayatu yenangu pansi pali olamuliliwa kuli Abishari mwana mwamuna wa Zeruia, mubale wa Yowabu, nafuti yenangu magulu yayatu pansi pali kulamuliwa Itai mu Gititi. ba mfumu bana kamba ku bankondo kuti, "Zo-ona nazayenda naimwe, ine mwine wake." 3 Koma mwamuna anakamba kuti, "Musayenda ku nkondo, pakuti tikataba sibazatifakako nzelu ise, kapena bena baise bafa sibazafako nzelu. Koma mulingana nama sausande ya ise! chaicho chizankala chabwino kuti munkale okonzekela kuti tandiza ku choka mu muzinda." 4 Pamene apo mfumu inabayanka kuti, "Nizachita chilichinse chamene chioneka bwino kuli imwe." Mfumu anaimili pa chiseko chamuzinda pamene ba nkondo bonse benzeli kuchoka muma handredi nama sausande. 5 Mfumu analamuli Yowabu, Abisha, na Ita kukamba kuti, "muchite pagnono na munyamata wamene alina Abisalomu." Bantu bonse bananvela kuti mfumu yapasa bazisogoleli lamulo yake pali Abisalomu. 6 Pamene apo bankondo banayenda ku mbali ya ziko pa Isilayeli, nkondo ina zala munsanga ya Eframu. 7 Bankondo bamu Isilayeli bana gonjesa kuja pamenso paba silikli ba Davide; kunali ku chekedwa kwa bazimuna bali twente sausande ija. 8 Nkondo ina zala konse ku mbali ya ziko ndipo bazimu bambili bamezewa na nsanga kudula na lupanga. 9 Chinachitika kuti Abisalomu ana kumanya ba silikali ba Davide. Abisalomu enzeli kuyenze bulu wake, ndiye bulu ina yenda pansi pantambi zikulu pamutengo wa oki ukulu, ndipo mutu waka unagwiliwa pa ntambi ya mutengo. Anasala alengela pakati pa kumwamba na pansi pamene bulu yamene enze kuyenza inapitiliza kuyenda. 10 Winangu anaona ichi naku uza Yowabu, Ona, Naona Abisalomu alelenga muutengo wa oki!" 11 Yowabu anakamba kuli mwamuna wamene anamuza va Abisalomu kuti, "Ona!wanu ona! Nichani chamene suna ugwesele pansi? sembe naku pasa Mashekeli ya siliva na chiomanga mumusana." 12 13 Mwamuna anamuyanka Yowabu kutu, "Ngankale kuti nalandila mashekele yali sausanda ya siliva, siningafikise kwanja yanga pa mwana wanfumu, chifukwa tanvela tonse pamene mfumu akulamulilani iwe, kulibe wamene azagwila munyamata Abisalomu.' Sembe naika umoyo wanga pa cha boza (ndiye kulib e chobisika kuchokela kuli mfumu). Sembe mwanilekelela ine." 14 Kuchoka apo Yowabu anakamba kuti, "sinizakuyembekezela iwe." Pamene apo Yowabu anatenga ntungo mumanja mwake naku ziponya pa mutima wa Abisalomu, pamene enzeli akali na moyo naku lelenga ku chokela mu mutengo wa oki. 15 Chokonkapo bamuna bafana bali teni bamene benze bana nyamula chida bana zunguluka Abisalomu, naku mumenya naku mupaya. 16 Chokonkapp Yowabu analiza lipenga, ndipo bankondo bana bwelela kuchokela kupilikisa a Isilayeli, popeza Yowabu anabwelesa bankondo bake. 17 Banamu tenga Abisalomu nakumu ponya muchimugodi chitali mu sanga; Bana shika tupi yake pause pamu mutolo ukuli wa myala, pamene a Isilayeli bonse bana taba, aliyense mwamuna kunyumba yake. 18 Manje Abisalomu, pamene enzeli na moyo, anabwela azimangila eka mwala ukulu ngati linga mu chigwa cha mfumu, popeza kuti anakamba, "Nilibe mwana mwamuna wamene anganyamule kukumbukiliwa lowa zina yanga." Lunga anaipasa zina yake. kufikila na lelo imaitaniwa kuti chikumbuso cha Abisalomu. 19 Kuchoka apo Ahimazi mwana mwamua wa Zadoki anakamba kuti, "Lekani ine nitamanga kuli mfumu yautenga wabwino, mwamene Yehova anamupulumusila kuchoka mumanja yaba dani bake." 20 Yowabu anamuyanka kuti, "Suzankala onyamula utenga lelo, ukachite pa siku inango. lelo suzanyamula utenga chifukwa mwana wamfumu afa. 21 Chokonkapo Yowabu anakaba kuli mu Chushiti kuti,"Yenda, kauze mfumu vamene waona." Mu Cushiti anazichepesa kwa Yowabu, naku tamanga. 22 Ndipo Ahimazi mwana mwamuna wa Zadoki anakamba futi kuli Yowabu, "Chilichonse chamene chinga chitike, npiempa kuti nitamange naku mukonka mu Cushiti." Yowabu anayanka, "nichani chamene ufunila kutamanga, mwana wanga mwamuna, paku ona kuti suatenga mpaso iliyonse pa utenga?" 23 "Chilichonse "chamene chizachitika," Ahimazi anakamba, "Nizatamanga." kuchoka apo Ahmazi anatamanga pa njila yaku dambo naku mupitilila mu Cushiti. 24 Manje Davide enzeli nkale pakati pongenela napo chokela pachiseko. Kamalonda anayenda pamwamba pa utenga wapa geti wa dippa naku nyamula menso yake Pamene analangana anaona mwamuna achita kufika, atamanga eka. 25 Kamalonda anakuwa naku uza mfumu, Kuchoa apo mfumu inakamba kuti, "Ngati ali eka, muli utenga mukamwa mwake. Wotamanga anabwela pafupi na mufupi namuzinda. 26 Kuchoka apo kamalonda anaona winangu mwamuna atamanga, ndipo kamulonda anaitana wonkala pa geti; anakamba kuti, "Ona, kuli mwamuna winangu wamene atamanga eka." Amfumu banakamba kuti, "Naye aleta utenga wabwino." 27 Pamene apo kamulonda anakamba kuti, "Niganiza monga kutamanga kwa mwamuna wamene ali pasogolo kuli monga kwa Ahimazi mwana mwamuna wa Zadoki. Amfumu banakamba kuti, "Nimwamuna wabwino ndipo abwela nautenga wabwino." 28 Kuchoka apo Ahimazi anaitana aku kamba kuli mfumu kuti, "Zonse zili bwino," Anazi chepesa pamenso pa mfumu na nkope yake pansi naku kamba kuti "Adalisike azimua bamene bana nyamula manja yabo pali iwe bwana wanga mfumu." 29 Pamene apo mfumu inayanka kuti, "Nanga zili bwino zonse na mwamuna mufana Abisalomu?" Ahimazi anayanka kuti, "Pamene Yowabu anituma ine, wanchito wanfumu kuli imwe, mfumu. naona kusokonezeka kwakulu, koma sininazibe kuti nichani." 30 Chokonkapo mfumu anakamba kuti, zungulukia pambali naku imililia apa." Pamene apo Ahimazi anazunguluka naku fendela pambali, naki imilila. 31 Pamene apa mu Cushiti anafka naku kamba kuti, "kuli utenga wabwino wa bwana wanga mfumu, popeza Yehova akubwezelani lelo kuchokela kuli bonse bamene bana ku nyamukilani." 32 Chokonkapo mfumu anakamba kuli mu Cushiti kuti, "Nanga zili bwino namunyamata mungona Abisalomu?" Mu Cushiti anayanka kuti, "Badani ba bwana wanga mfumu, na bonse bamene bana kunyamukilani ku ononga imwe, bafunika kunkala monga mwamene uja munyamata alili." 33 Kuchoka apo mfumu inankala nachisoni, nakuyenda ku malo pa mwamba pa geti naku lila maninigi pamene enzeli kuyenda analilia, "mwana wanga mwamuna, mwana wanga mwamuna Abisalomu! Bansembe nenze nafa ndine mumalo mwako, Abisalomu, mwana wanga mwamuna, mwamuna wanga mwamuna.